Zef. 2 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Aŵauza anthu kuti alape.

1Inu anthu opanda manyazinu,

chitani msonkhano, mulape,

2adani asanakumwazeni ngati mungu,

ukali woopsa wa Chauta usanakugwereni,

tsiku la mkwiyo wa Chauta lisanakupezeni.

3Funafunani Chauta, inu nonse odzichepetsa,

inu amene mumamvera malamulo ake.

Chitani zolungama, khalani odzichepetsa.

Mwina mwake mudzatha kupulumuka

pa tsiku la mkwiyo wa Chauta.

Mulungu adzaononga maiko oyandikana ndi Yuda

4

Mau a Chauta akukudzudzulani,

inu anthu a ku Kanani, dziko la Afilisti,

akuti, “Ndidzakuwonongani nonse

sipadzatsala ndi mmodzi yemwe.”

6Dziko limene lili m'mphepete mwa nyanja,

lidzasanduka madambo a abusa,

ndi makola a nkhosa.

7Kumeneko kudzakhala dziko la otsala a m'banja la Yuda.

Azidzadyetsa nkhosa zao m'mbali mwanyanjamo,

ndipo madzulo azidzagona ku nyumba za ku Asikeloni.

Pakuti Chauta, Mulungu wao adzaŵasamalira,

ndiye amene adzaŵabwezere ufulu wao.

Za Amowabu ndi Aamoni

8 Yes. 15.1—16.14; 25.10-12; Yer. 48.1-47; Ezek. 25.8-11; Amo. 1.13-15; Yer. 49.1-6; Ezek. 21.28-32; 25.1-7; Amo. 1.13-15 Chauta akuti,

“Ndamva kunyoza kwa Amowabu,

ndiponso kutukwana kwa Aamoni,

m'mene anyozera anthu anga

ndi m'mene adzikuzira m'dziko mwao.

9 Gen. 19.24 Nchifukwa chake Ine Chauta Wamphamvuzonse

ndikulumbira kuti,

Pali Ine ndemwe, Mulungu wamoyo wa Israele,

Amowabu adzaonongedwa ngati anthu a ku Sodomu,

Aamoni adzaonongedwa ngati anthu a ku Gomora.

Malowo adzakhala ngati dera la zitsamba za

khwisa ndi la nkhuti za mchere,

dziko lachipululu mpaka muyaya.

Otsala mwa anthu anga adzafunkha malowo.

Opulumuka a mtundu wanga adzalandira

malowo ngati dziko lao.”

10Chimenechi chidzakhala chilango

choyenerera kunyada kwaoko,

chifukwa adanyoza anthu a Chauta Wamphamvuzonse.

11Motero Chauta adzaŵaopsa kwambiri.

Adzaononga milungu yonse ya pa dziko lapansi.

Mitundu yonse ya anthu idzampembedza Chauta,

mtundu uliwonse ku dziko lakwao.

Za Etiopiya ndi Asiriya

12 Yes. 18.1-7 Inunso Aetiopiya,

Chauta adzakukanthani ndi lupanga lake.

13 Yes. 10.5-34; 14.24-27; Nah. 1.1—3.19 Chauta adzasamulira dzanja lake kumpoto

ndi kuwononga dziko la Asiriya.

Mzinda wa Ninive adzausandutsa bwinja,

udzakhala wagwaa ngati chipululu.

14Choncho zoŵeta zizidzagona kumeneko

chimodzimodzinso nyama zonse zakuthengo.

Adembo ndi akanungu azidzagona pa makapotolosi ake.

Akadzidzi azidzalira pa windo,

ndipo makwangwala azidzakhala pa bwalo lake.

Mitengo yake yamkungudza adzaisadza.

15Umenewo ndiwo mzinda

umene unkadzimva kuti ndi wokhazikika,

umene mumtima mwake unkati,

“Ine pano! Palibenso wina ai!”

Tauwonani m'mene wasakazikira tsopano!

Wasanduka bwinja lokhalamo nyama zakuthengo.

Aliyense wodutsamo

azidzangotsonya nkumapukusa mutu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help