1Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, chaka chachisanu ndi chimodzi cha ukapolo, ndidaali khale m'nyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Mwadzidzidzi mphamvu za Ambuye Chauta zidandifikira.
2
15Chauta adati, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziwona zimenezi? Komabe udzaona zonyansa zina zazikulu kupambana zimenezi.”
16Kenaka adapita nane ku bwalo lam'kati la Nyumba ya Chauta. Kumeneko, ku khomo loloŵera ku Nyumba ya Chauta, pakati pa khonde ndi guwa, kunali anthu aamuna ngati 25. Adaafulatira Nyumba ya Chautayo, nkhope zao zitaloza chakuvuma, ndipo ankapembedza dzuŵa choyang'ana kuvuma.
17Chauta adandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziwona zimenezi? Ayuda sakukhutira nazo zonyansa akuchita panozi. Koma akufalitsanso zandeu m'dziko lonse. Motero akuutsa ukali wanga, akundipsetsa mtima ndi zochita zao.
18Tsono Ine ndidzaŵalanga ndili wokwiya. Sindidzaŵayang'ana ndi maso achifundo, ndipo sindidzaŵalekerera. Ngakhale adzalire mofuula kwa Ine, sindidzaŵamvera ai.”
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.