Nyi. 3 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1Usiku uliwonse ndili gone pabedi panga

ndinkangomufunafuna amene mtima wanga umamkonda.

Ndidamufunafuna koma osampeza.

Ndidamuitana, koma iye osandiyankha.

2Ndiye ndidati,

“Ai, tsopano ndidzuka ndi kuloŵa mu mzinda,

m'miseu ndi m'mabwalo.

Ndimufunafuna amene mtima wanga umamkonda.”

Ndidamufunafunadi, koma osampeza.

3Alonda adandipeza

pamene ankayendera mzinda.

Ndidaŵafunsa kuti,

“Kodi mwandiwonerako amene mtima wanga umamkonda?”

4Ndidangoti iwo aja ntaŵapitirira pang'ono,

ndampeza amene mtima wanga umamkonda.

Ndidamgwira, osamlola kuti achoke,

mpaka nditamloŵetsa m'nyumba ya amai anga,

m'chipinda cha amene adandibala.

5Inu akazi a ku Yerusalemu,

ndithu ndakupembani,

pali mphoyo ndi nswala zakuthengo,

chikondichi musachigwedeze kapena kuchiwutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

Nyimbo Yachitatu.

Mkazi

6Kodi nchiyaninso icho

chikutulukira ku chipululucho

ngati utsi watolotolo,

chonunkhira mure ndi lubani,

chokhala ndi zonunkhira zonse

zogulitsa anthu amalonda?

7Amenewo ndi machira a Solomoni.

Pali ankhondo makumi asanu ndi limodzi,

amuna anyonga a ku Israele operekeza.

8Onsewo agwira malupanga,

ndipo ngodziŵa kumenya nkhondo,

aliyense wavala lupanga pambali pake,

kuti alimbane ndi aupandu usiku.

9Mfumu Solomoni adadzipangira machira

a matabwa a ku Lebanoni.

10Milongoti yake adapanga yasiliva,

kumbuyo kwake kunali kwagolide,

pampando pake panali nsalu yofiirira.

11Tulukani, inu akazi a ku Ziyoni,

mudzaone Mfumu Solomoni,

atavala chisoti chaufumu

chimene mai wake adamuveka

pa tsiku la ukwati wake,

tsiku limene mtima wake unkasangalala.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help