Mas. 127 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kutamanda ubwino wa MulunguNyimbo ya Solomoni yoimba pokwera ku Yerusalemu.

1Chauta akapanda kumanga nawo nyumba,

omanga nyumbayo angogwira ntchito pachabe.

Chauta akapanda kulonda nawo mzinda,

mlonda angochezera pachabe.

2Mungodzivuta nkulaŵirira m'mamaŵa

ndi kukagona mochedwa,

kugwira ntchito movutikira kuti mupeze chakudya.

Paja Chauta amapatsa okondedwa ake zosoŵa zao

iwowo ali m'tulo.

3Zoonadi, ana ndi mphatso yochokera kwa Chauta,

zidzukulu ndi mphotho yake.

4Ana apaunyamata ali ngati mivi m'manja

mwa munthu wankhondo.

5Ngwodala amene phodo lake nlodzaza ndi mivi yotere.

Sadzamchititsa manyazi

akamalankhula ndi adani ake pa bwalo lamilandu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help