Mas. 123 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pemphero lopempha chifundoNyimbo yoimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndikukweza maso anga kwa Inu,

Inu amene mumakhala pa mpando wachifumu kumwamba.

2Monga momwe anyamata amayang'anira

ku dzanja la bwana wao,

monga momwe adzakazi amayang'anira

ku dzanja la dona wao,

ndi momwenso timayang'anira ife

kwa Chauta Mulungu wathu,

mpaka atatichitira chifundo.

3Mutichitire chifundo, Inu Chauta,

mutichitire chifundo,

pakuti adani athu atinyoza kopitirira malire.

4Pa nthaƔi yaitali,

anthu olemera akhala akutinyodola,

anthu onyada akhala akutinyoza.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help