Mas. 15 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Khalidwe lokomera MulunguSalmo la Davide.

1Inu Chauta, kodi ndani angathe kukhala m'Nyumba mwanu?

Ndani angathe kukhala pa phiri lanu loyera?

2Ndi munthu amene amayenda mosalakwa,

amene amachita zolungama nthaŵi zonse,

amene amalankhula zinthu ndi mtima woona.

3Ndi amene sasinjirira ndipo sachita anzake zoipa,

kapena kumafalitsa mbiri yoipa ya anzake.

4Ndi amene amanyoza munthu womkana Mulungu,

koma amalemekeza anthu omvera Chauta.

Ndi amene amachitadi zimene walonjeza,

ngakhale zikhale zoŵaŵa chotani.

5Ndi amene sakongoza ndalama zake

kuti alandire chiwongoladzanja,

amene salandira chiphuphu

kuti azunze munthu wosalakwa.

Munthu wochita zimenezi,

palibe chilichonse chimene chidzamgwedeze.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help