Tob. 13 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nyimbo ya Tobiti

1Tsono Tobiti adayamika Mulungu, nati,

“Atamandike Mulungu wamuyaya

chifukwa ufumu wake ndi wosatha.

2Iye amalanga, ndiponso amakhululukira.

Amafikitsa anthu ku dziko la akufa,

komanso amaŵatulutsa ku manda.

Palibe munthu amene angathe kuthaŵa dzanja lake.

3Ana a Israele, tamandani Mulungu,

muyamikeni pamaso pa mitundu ina ya anthu.

Chifukwa ngati adakumwazani

pakati pa anthu a mitundu ina,

4 Yes. 63.16; Yer. 3.4; Lun. 14.3; Mphu. 23.1, 4; Mt. 6.9 kumenekonso adakuwonetsani ukulu wake.

Muyamikeni pamaso pa anthu onse.

Iwowo ndi Ambuye athu,

Iwo ndi Mulungu wathu,

Iwo ndi Atate athu,

ndipo ndi Mulungu mpaka wamuyaya.

5“Angakhale amakulangani

chifukwa cha machimo anu,

adzakuchitirani chifundo nonsenu,

adzakusonkhanitsani

kuchokera ku mitundu yonse ya anthu

kumene adakumwazirani.

6Ngati mutembenukira kwa Iye

ndi mtima wanu wonse ndi nzeru zanu zonse,

pokhala okhulupirika pamaso pake,

ndiye kuti adzabwerera kwa inu

ndipo sadzakufulatiraninso.

Onani zimene adakuchitirani,

muzimuyamika mokweza mau.

Tamandani Ambuye achilungamo,

lemekezani Mfumu ya mibadwo yonse.

“Ine m'dziko la ukapolo lino

ndimayamika Mulungu,

ndimakamba za mphamvu zake zazikulu

kwa mitundu ya anthu ochimwa.

Anthu ochimwanu,

bwererani kwa Iye

ndi kuchita zolungama pamaso pake.

Mwina adzakukomerani mtima

ndi kukuchitirani chifundo.

7Ine ndimayamika Mulungu wanga,

mtima wanga umakondwerera kwambiri

Mfumu yakumwamba.

8Anthu onse azilalika ulemerero wake

ndi kumuimbira nyimbo zomutamanda mu Yerusalemu.

9 Yes. 60.1-22; Chiv. 21.9—22.5 “Iwe Yerusalemu, mzinda woyera,

udalangidwa chifukwa cha zoipa za anthu ako.

Koma anthu olungama adzaŵachitiranso chifundo.

10Uzithokoza Ambuye monga kuyenera,

uzitamanda Mfumu yamuyaya,

ndipo Nyumba ya Mulungu aimangenso mwa iwe,

kuti ukhale ndi chimwemwe.

Mwa iwe Mulungu asangalatsenso onse

amene ali ku ukapolo.

Mwa iwe akonde onse ovutika

pa mibadwo yonse yakutsogolo.

11“Kuŵala kwako kudzaŵala kwambiri

pa maiko onse a m'dziko lino lapansi.

Mitundu yambiri ya anthu idzafika

kuchokera kutali ku mathero onse

a dziko lino lapansi.

Idzatamanda dzina loyera la Ambuye Mulungu

izidzapereka mphatso kwa Mfumu yakumwamba.

Mwa iwe mibadwo yonse idzasangalala,

ndipo dzina la mzinda wosankhidwawe

lidzakumbukika pa mibadwo yonse yakutsogolo.

12“Atembereredwe onse amene adzakunyoza,

onse amene adzakuwononga

ndi kugwetsa makoma ako,

onse amene adzagwetsa nsanja zako

ndi kutentha nyumba zako.

Koma akhale odala nthaŵi zonse

amene adzakumanganso.

13Pamenepo iwe udzakondwa ndi kusangalala,

chifukwa ana ako olungama adzasonkhana pamodzi,

ndipo adzatamanda Ambuye mpaka muyaya.

14“Ngodala anthu amene amakukonda,

amene amakondwerera mtendere wako.

Ngodala amene adakumvera chisoni

pamene unali pa mavuto,

chifukwa adzakondwa nawe

adzasangalala nawe mpaka muyaya.

15Mtima wanga utamande Ambuye

Mfumu yaikulu,

16chifukwa Yerusalemu adzamangidwanso

kuti ukhale mzinda waowao mpaka muyaya.

“Ndidzakondwa ngati mwa anthu anga

adzatsalako ena kuti adzaone ulemerero wako

ndi kuthokoza Mfumu ya Kumwamba.

Zitseko za Yerusalemu adzazipanga

ndi miyala ya safiro ndi ya emeradi,

nsanja zake adzazipanga ndi golide,

malinga akenso adzapangidwa ndi golide weniweni.

17Miseu ya Yerusalemu adzaikonza

ndi miyala ya rubi,

ndiponso miyala ina yamtengowapatali ya ku Ofiri.

M'zipata za ku Yerusalemu adzaimba mosangalala,

ndipo mabanja onse am'menemo adzaimba kuti,

‘Aleluya! Atamandike Mulungu wa Israele.’

Mwa iwe anthu onse adzatamanda dzina loyera

la Mulungu mpaka muyaya.”

Nyimbo yoyamika ya Tobiti idathera pomwepo.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help