Miy. 28 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za munthu woipa mtima ndi munthu wolungama

1Woipa mtima amangodzithaŵira

popanda wina wompirikitsa,

koma wochita zabwino amalimba mtima ngati mkango.

2Eni dziko akachita zaupandu, oŵalamulira amachuluka.

Koma anthu akakhala omvetsa ndi odziŵa zinthu,

dzikolo limakhazikika nthaŵi yaitali.

3Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake,

ali ngati mvula yamkuntho

yosasiya konse chakudya m'minda.

4Amene samvera malamulo amatamanda anthu oipa mtima,

koma otsata malamulo amatsutsana nawo.

5Anthu oipa samvetsa kuti chilungamo nchiyani,

koma amene amatsata kufuna kwa Chauta

amachimvetsa kwathunthu.

6Munthu wosauka amene amayenda mwaungwiro

amaposa kwambiri munthu wolemera amene ali wonyenga.

7Amene amatsata malamulo ndiye mwana wanzeru,

koma amene amayenda ndi anthu adyera,

amachititsa atate ake manyazi.

8Amene amachulukitsa chuma chake

polandira chiwongoladzanja ndi pochikundika,

chumacho amachikundikira ena amene

adzachitira chifundo anthu osauka.

9Wina akamakana kumvera malamulo,

ngakhale mapemphero ake amanyansira Mulungu.

10Amene amasokeza anthu olungama

kuti azitsata njira yoipa, adzagwa m'dzenje lake lomwe.

Koma anthu amene alibe cholakwa

adzalandira choloŵa chabwino.

11Munthu wolemera amadziyesa wanzeru,

koma munthu wosauka amene ali womvetsa zinthu,

amamtulukira.

12Anthu abwino akapambana,

pamakhala chikondwerero chachikulu,

koma oipa mtima akalandira ulamuliro, anthu amabisala.

13Wobisa machimo ake sadzaona mwai,

koma woulula ndi kuleka machimo, adzalandira chifundo.

14Ndi wodala munthu amene amaopa Chauta nthaŵi zonse,

koma woumitsa mtima wake adzagwa m'tsoka.

15Monga muja umakhalira mkango wobangula

kapena chimbalangondo cholusa,

ndimonso imakhalira mfumu yoipa mtima kwa anthu osauka.

16Wolamulira amene samvetsa zinthu

amapondereza anthu mwankhanza,

koma wodana ndi phindu loipa amatalikitsa masiku ake.

17Munthu amene wapalamula mlandu wopha mnzake,

akhale womathaŵathaŵa mpaka kufa kwake.

Wina aliyense asamthandize.

18Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa,

koma woyenda mokhotakhota adzagwa m'dzenje.

19Wolima m'munda mwake adzakhala ndi chakudya chambiri,

koma wonka nafuna zopanda pake adzasauka kwambiri.

20Munthu wokhulupirika adzakhala ndi madalitso ambiri,

koma wofunitsitsa kulemera msanga

sadzalephera kupeza chilango.

21Kuchita tsankho si kwabwino,

komabe ena amaweruza mokondera

chifukwa cha kachidutswa ka buledi.

22Munthu wakaliwumira amafunitsitsa kulemera mofulumira,

koma sadziŵa kuti umphaŵi udzamgwera.

23Amene amadzudzula mnzake,

potsiriza pake mnzakeyo adzamkonda kwambiri

kupambana amene ali ndi mau oshashalika.

24Wobera atate ake kapena amai ake

namanena kuti kutero sikulakwa,

ameneyo ndi mnzake wa munthu woononga.

25Munthu waumbombo amautsa mkangano,

koma wokhulupirira Chauta adzalemera.

26Samvazaanzake nchitsiru,

koma wotsata nzeru za ena adzapulumuka.

27Amene amapatsa osauka sadzasoŵa kanthu

koma amene amatsinzina dala kuti asaŵapenye,

adzatembereredwa kwambiri.

28Anthu oipa mtima akalandira ulamuliro,

anthu amabisala,

koma oipawo akaonongeka,

anthu ochita chilungamo amapeza bwino.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help