Mas. 128 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mphotho ya kumvera ChautaNyimbo yoimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ngwodala aliyense woopa Chauta,

amene amayenda m'njira zake.

2Udzadya zimene manja ako adagwirira ntchito.

Udzasangalala, ndipo zinthu zidzakuyendera bwino.

3Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka,

m'kati mwa nyuma yako.

Ana ako adzakhala ngati tiziphukira taolivi,

kuzungulira tebulo lako.

4Zoonadi, ndimo m'mene adzakhalire wodala

munthu woopa Chauta.

5Chauta amene amakhala ku Ziyoni akudalitse.

Uwone m'mene Yerusalemu zinthu zidzamuyendere bwino

masiku onse a moyo wako.

6Ukhale ndi moyo wautali

kuti uwone zidzukulu zako.

Mtendere ukhale ndi Israele.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help