Lun. 10 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Zimene luntha lidaŵachitira anthu akale

1 Gen. 1.26-28 Luntha linkasunga munthu woyamba,

tate wa mtundu wa anthu,

pamene anali yekha, Mulungu atamulenga.

Munthuyo atachimwa, luntha lidamupulumutsa,

2ndipo lidamupatsa mphamvu

zolamulira zolengedwa zonse.

3 Gen. 4.8-13 Koma pamene wina wosalungama

adasiyana ndi luntha mwaukali,

adaonongeka chifukwa cha kupha

mbale wake mwachipseramtima.

4 Gen. 7.1—8.22 Pamene dziko lino lapansi lidaamira m'madzi

chifukwa cha iyeyo,

luntha lidaapulumutsa dzikolo

poongolera olungama aja

pa mtengo wachabechabe.

5 Gen. 11.1-9; 12.1-3; 22.1-19 Pamene mitundu ya anthu idasokonezeka

itapangana kuti ichite choipa,

luntha lidapatulapo munthu

amene anali wolungama,

nkumusunga wopanda cholakwa pamaso pa Mulungu.

Lidamulimbitsanso kuti angafooke

ndi chisoni chomvera mwana wake.

6 Gen. 19.1-29 Luntha lidapulumutsanso munthu wina wolungama

pamene anthu oipa adaonongeka.

Iyeyo adathaŵa moto umene udagwa pa mizinda isanu ija.

7Mboni ya kuipa kwao ndi nthaka youma

imene sileka kufuka utsi,

imene mbeu zake zimabereka zipatso zimene sizipsa.

Ndipo chipilala chamchere chili pompo chikhalire,

ngati chikumbutso cha mtima wosakhulupirira.

8Anthuwo atasiyana ndi luntha,

sadathenso kuzindikira zabwino,

koma adasiyira amoyo mbiri ya kupenga kwao,

kuti zolakwa zao zizikumbukika nthaŵi zonse.

9Koma luntha lidapulumutsa atumiki ake

m'zovuta zao.

10 Gen. 27.43; 28.10-22; 32.24-30 Munthu wolungama uja amene ankathaŵa

ukali wa mbale wake,

lidamuwongolera pa njira zolungama.

Lidamuwonetsa ufumu wa Mulungu

ndi kumudziŵitsa zinthu zoyera.

Lidamupambanitsa pa ntchito zake zoŵaŵa

ndipo lidachulukitsa phindu la ntchito zake.

11Lidamutchinjiriza pakati pa anthu

ofuna kumchenjerera,

ndipo lidamulemeretsa.

12Lidamuteteza kwa adani ake,

ndipo lidamupulumutsa pakati pa anthu

ofuna kumutchera misampha.

Lidamupambanitsa pa ndeu yolimbana koopsa,

kuti aphunzire kuti kutumikira Mulungu

kumalimbitsa munthu kupambana zonse.

13 Gen. 37.12-36; 39.1-23; 41.37-44 Munthu wina wolungama atagulitsidwa

luntha silidamusiye,

lidamutchinjiriza kuti asachimwe.

Lidaloŵa naye ndi m'ndende momwe.

14Silidamusiye ali m'maunyolo,

koma lidamupatsa ndodo yaufumu

ndi mphamvu zolamulira

eni ake ovuta a dzikolo.

Anthu amene ankamuneneza,

lidaŵatsutsa kuti ndi abodza,

kenaka lidamupatsa ulemu wamuyaya.

Mulungu alezera mtima Ejipito

15 Eks. 1.1—15.21 Luntha lidapulumutsa

anthu oyera mtima ndi osachimwa

kwa mtundu wa anthu oŵazunza.

16Lidaloŵa mu mtima wa mtumiki wa Ambuye,

ndipo lidachita zizindikiro ndi zozizwitsa

polimbana ndi mafumu oopsa.

17Anthu oyera mtima lidaŵapatsa malipiro

a ntchito zao zoŵaŵa,

lidaŵaongolera pa njira yodabwitsa.

Masana linali ngati mthunzi wao,

usiku linali ngati chilangali

choŵala ngati nyenyezi.

18Lidaŵaolotsa Nyanja Yofiira,

ndi kuŵapititsa pakati pa madzi ozama.

19Lidamiza adani ao pansi pa nyanja,

kenaka nkuŵavuulira ku mtunda.

20Motero anthu olungama adafunkha chuma

cha anthu osamva aja.

Adaimbira dzina lanu loyera Inu Ambuye,

onse ndi mtima umodzi

adatamanda dzanja lanu loŵateteza.

21Luntha lidatsekula pakamwa

pa anthu osalankhula,

lidamasula lilime la ana akhanda.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help