Yes. 3 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chipwirikiti mu Yerusalemu

1Tsopano Ambuye, Chauta Wamphamvuzonse,

ali pafupi kulanda Yerusalemu ndi Yuda

chithandizo cha mtundu uliwonse

chimene anthu amadalira.

Adzachotsa chakudya chonse,

adzachotsa madzi onse,

2anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo,

aweruzi ndi aneneri,

olosa ndi akuluakulu,

3atsogoleri ankhondo ndi anthu olemekezeka,

aphungu ndi amatsenga,

ndiponso akatswiri a njirisi.

4Adzaŵaikira anyamata kuti akhale mafumu ao,

ndipo ana amakanda ndiwo adzaŵalamulira.

5Anthu adzazunzana,

aliyense adzazunza mnzake.

Anyamata adzachita chipongwe akuluakulu,

ndipo anthu achabechabe adzanyoza olemekezeka.

6Munthu adzagwira mbale wake

m'nyumba ya atate ao,

nkunena kuti,

“Iwe uli nawo mwinjiro,

ndiye ukhale mtsogoleri wathu

nthaŵi yamavutoyi.”

7Tsiku limenelo mbale wakeyo adzayankha kuti,

“Ine ai toto! Mavuto otereŵa

ndilibe mankhwala ake,

m'nyumba mwanga momwe ndilibe chakudya kapena chovala.

Musaike ine kuti ndikhale

mtsogoleri wa anthu.”

8Zoonadi Yerusalemu akusakazika ndipo Yuda akugwa,

chifukwa zokamba ndiponso ntchito

za anthu am'menemo nzonyoza Chauta.

Salabadako za ulemerero wa Mulungu.

9Maonekedwe a nkhope zao amaŵatsutsa.

Amachimwa poyera ngati m'mene ankachitira

anthu a mu Sodomu, sabisa konse.

Tsoka kwa iwowo, achita kudziputira okha mavuto.

10Ngodala anthu omvera Mulungu

pakuti zinthu zidzaŵayendera bwino,

adzakondwera ndi phindu la ntchito zao.

11Koma tsoka kwa anthu oipa!

Zinthu zidzaŵaipira.

Zimene akhala akuchitira anzao

zomwezo zidzaŵabwerera.

12Inu anthu anga,

amene akukuponderezani ndi ana chabe,

ndipo amene akukulamulani ndi akazi.

Aah! Anthu anga,

atsogoleri anu akukusokeretsani,

akukusokonezerani njira zanu.

Chauta aweruza anthu ake

13Tsopano Chauta afuna kuyambapo mlandu,

wakonzeka kale kuweruza anthu ake.

14Chauta akuŵaimba mlandu

akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake.

Akuŵazenga kuti,

“Ndinu amene mwaononga munda wanga wamphesa.

Nyumba zanu zadzaza ndi zinthu zolanda kwa amphaŵi.

15Mukuŵapsinjiranji anthu anga?

Chifukwa chiyani mukuŵadyera masuku pamutu amphaŵi?”

Akutero Ambuye, Chauta Wamphamvuzonse.

Achenjeza akazi a ku Ziyoni

16Chauta adati,

“Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri:

amayenda makosi ali wee,

amayang'ana ndi maso ophika.

Amayenda nyang'anyang'a

ndi kuliza zigwinjiri zam'miyendo.

17Nchifukwa chake Ambuye adzatulutsa

zipere kumutu kwa akazi a ku Ziyoniwo,

tsitsi lao lonse lidzatha phu!”

18Tsiku limenelo Ambuye adzaŵachotsera zokongoletsera m'miyendo, kumutu ndi m'khosi,

19maukufu, makoza, ndi nsalu zakumaso,

20maduku, zigwinjiri, malamba, mabotolo a zonunkhira, zithumwa,

21mphete, zipini,

22madelesi apaphwando, makepi, miinjiro, zikwama,

23akalilole, zovala zabafuta, nduŵira, ndiponso nsalu zam'mapewa.

24M'malo mwa kununkhira padzakhala kununkha,

m'malo mwa lamba adzavala chingwe,

m'malo mwa tsitsi lopesa bwino

adzakhala ndi mipala,

m'malo mwa delesi la mtengo wapatali

adzavala chiguduli,

m'malo mwa kunyadira kukongola

adzachita manyazi.

25Iwe Yerusalemu, anthu ako aamuna

adzaphedwa ndi lupanga,

ndipo anthu ako amphamvu adzafera ku nkhondo.

26Choncho pa zipata zako

padzakhala kulira kokhakokha,

iweyo udzasakazidwa nkukhala pansi,

ukuvimvinizika pa fumbi.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help