Lun. 14 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mafano osema kuyerekeza ndi chombo cha Nowa

1Wina pokonzekera kuwoloka nyanja yaukali,

amapemphera mtengo umene uli wofooka

kupambana chombo chomwe chamunyamula.

2Chombo adachiganiza ndi munthu wofuna phindu,

mmisiri wanzeru, nkuchipanga ndi luso.

3Koma inu Atate, ndi chisamaliro chanu

chimene chimayendetsa chombocho,

poti ndinu amene mudachipatsa njira pakati pa nyanja

ndiponso khwalala labwino pakati pa mafunde.

4Choncho mudatiwonetsa kuti

mungathe kutipulumutsa m'mavuto aliwonse,

kotero kuti ngakhale munthu wopanda luso lake

angathe kuyenda pa nyanja.

5Simufuna kuti ntchito za nzeru zanu

zikhale zopanda phindu.

Choncho anthu saopa imfa

ngakhale atakwera m'kabwato kofooka,

amapita pa mafunde atakwera m'kabwato,

mpaka kukafika ku mtunda.

6Pajatu ngakhale pachiyambi paja

pamene ziphona zonyada zinkatayika,

chikhulupiriro cha dziko lonse chidathaŵira m'chombo.

Ndipo mutayendetsa chombocho ndi dzanja lanu,

mudalisiyira dziko lapansi

mbeu ya anthu a mbadwo watsopano.

7Zoonadi, ndi wotamandika mtengo

wodzetsa chilungamo.

8Koma litembereredwe fano

lopangidwa ndi manja a munthu,

pamodzi ndi mmisiri wake yemwe,

poti ndiye adalipanga ndi kutchula mulungu

chinthu chimene chimaola.

9Mulungu amadana ndi anthu osamvera,

amaipidwa nako kusamvera kwao.

10Pajatu chinthu chimene chidapangidwacho

chidzalangidwira kumodzi ndi wochipanga.

11Nchifukwa chake mafano a mafuko ena

nawonso Mulungu adzaŵaononga,

pakuti ngakhale adapangidwa

ndi chinthu cholengedwa ndi Mulungu,

amalakwitsa mitima ya anthu,

ndiponso amakhala misampha yokola anthu opusa.

Chiyambi cha kupembedza mafano

12Ganizo lopanga mafano

ndiye chinali chiyambi cha dama limenelo.

Moyo wa anthu udaonongeka

chifukwa chakuyamba kupanga zoterezi.

13Pa chiyambi kunalibe mafano,

ndipo sikuti adzakhalapo mpaka muyaya.

14Mafano adabwera pansi pano

ndi anthu okhulupirira zachabe,

nchifukwa chake Mulungu adaŵakonzera

zoti aonongeke msanga.

15Bambo wina akuvutika ndi maliro a mwana wake,

adapanga chithunzi cha mwanayo

amene Mulungu adamtenga mwadzidzidzi.

Chimene dzuloli chinali mtembo chabe,

adayamba kuchipembedza ngati mulungu,

ndipo adasiyira a m'nyumba mwake

miyambo yachinsinsi,

yachipembedzo ndi yachinamwali.

16Tsono ndi nthaŵi mazoloŵero oipawo adalimbika,

nasanduka ngati lamulo,

ndipo mafumu adalamula

kuti anthu azipembedza zithunzi zosemasema.

17Amene sankatha kulemekeza mafumu pamaso pao,

chifukwa choti anali kutali,

ankayesetsa kukumbukira nkhope yao.

Ndipo ankapanga chithunzi chofanafana ndi mfumu

imene ankafuna kuilemekezayo.

Choncho munthu amene ankakhala naye kutali,

ankamlambira monga ngati ali naye pafupi.

18Kudzikuza kwa mmisiri kudakakamiza

anthu osaidziŵa mfumuyo

kuti afalitse chipembedzo chake.

19Iyeyo pofuna kukomera mfumuyo,

adayesetsa ndithu kukometsa chithunzicho.

20Tsono anthu ambirimbiri

atakopeka ndi luso la ntchito yake,

adayamba kuipembedza ngati mulungu

mfumu yomwe poyamba

ankangoilemekeza ngati munthu.

21Zimenezi anthu adakodwa nazo mu msampha,

pakuti chifukwa cha matsoka

kapena malamulo a mfumu,

anthuwo ankatcha mwala kapena mtengo

dzina lopatulika.

Zotsatira za kupembedza mafano

22Pambuyo pake sikudakwanire kuti iwowo asokere

posadziŵa zoona za Mulungu,

koma ankakhalanso pa nkhondo yoopsa

chifukwa cha kusadziŵako,

ndipo tsoka lotere ankalitcha mtendere.

23Chifukwa cha kupereka ana ao ku nsembe,

kapena kuchita miyambo yachinsinsi ija,

kapena kulola madyerero

pamodzi ndi zokondweretsa zonyansa,

24sankathanso kusunga ungwiro

pa moyo wao ndi pa maukwati ao.

Mwina munthu ankapha mnzake monyenga,

mwina kumuvuta pochita chigololo ndi mkazi wake.

25Ponseponse panali chisokonezo:

magazi, kupha anthu,

mabodza ndi kuchenjerera ena,

kuipiratu, kusakhulupirirana,

phokoso ndi kulumbira zonama.

26Ankasokoneza anthu abwino,

sankathokoza polandira zabwino,

ankaipitsa mitima, ankachita zadama zamtundu,

ndipo pa chikwati ankachita zosayenera,

chigololo ndi zonyansa zina.

27Chipembedzo cha mafano osatchulika,

ndiye chiyambi cha zoipa zonse,

gwero lake ndi mathero ake.

28Anthu oŵapembedza mafanowo

amasangalala kopengetsa,

mwina amalosa zabodza.

Mwina amachita zosalungama

mwina amaphwanya msanga malonjezo olumbira.

29Popeza kuti amakhulupirira mafano opanda moyo,

saopa kuti nkupeza mavuto

chifukwa cha malumbiro ao onama.

30Koma chilango chidzaŵagwera

chifukwa cha zinthu ziŵiri:

Chifukwa adalakwira Mulungu kwakukulu

potsata mafano,

ndiponso chifukwa adachita monyenga

malumbiro oipa, kunyoza chilungamo.

31Chimene chimalondola tchimo la munthu wosalungama

si mphamvu za zinthu zimene amazitchula polumbira,

koma ndi chilango choyenera

chimene chimagwera anthu ochimwawo.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help