Mas. 70 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pemphero lopempha chithandizo(Mas. 40.13-17)Kwa Woimbitsa Nyimbo. Salmo la Davide la Chikumbutso.

1Inu Mulungu, pulumutseni.

Inu Chauta, fulumirani kudzandithandiza.

2Anthu ofunafuna moyo wanga,

muŵachititse manyazi ndi kuŵasokoneza.

Amene akhumba kundipweteka,

abwezedwe m'mbuyo ndi kunyozedwa.

3Amene amandinyodola kuti, “Ha, Ha,”

achoke ndi manyazi poona kuti alephera.

4Koma onse okufunafunani

akondwe ndi kusangalala chifukwa cha Inu.

Onse okondwerera chipulumutso chanu,

azinena kosalekeza kuti,

“Chauta ndi wamkulu.”

5Inu Chauta, ine ndine wolefuka ndi wosoŵa,

bwerani msanga kwa ine, Inu Mulungu.

Inu ndinu mthandizi wanga ndi Mpulumutsi wanga.

Inu Mulungu wanga, musachedwe kudzandithandiza.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help