Mas. 121 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nyimbo yoimba pokwera ku Yerusalemu

1Ndimakweza maso anga ku mapiri.

Kodi chithandizo changa chimachokera kuti?

2Chithandizo changa nchochokera kwa Chauta,

amene adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

3Sadzalola phazi lako kuti literereke,

Iye amene amakusunga sadzaodzera.

4Zoonadi, amene amasunga Israele,

ndithu sadzaodzera kapena kugona.

5Chauta ndiye amene amakusunga,

Chauta ndiye mtetezi wako

ali ku dzanja lako lamanja.

6DzuƔa silidzakupweteka masana,

mwezi sudzakuvuta usiku.

7Chauta adzakuteteza ku zoipa zonse,

adzasamala moyo wako.

8Chauta adzakusunga kulikonse kumene udzapita,

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help