Lun. 5 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1Tsono munthu wolungama adzaima osaopa kanthu

pamaso pa anthu amene ankamusautsa

ndi amene ankanyazitsa kulimbika kwake.

2Pomuwona adzanjenjemera ndi mantha oopsa,

adzadabwa poona kupulumuka kwake kosayembekezeka.

3Ndi nthumanzi mumtima mwao,

ndiponso movutika ndi moŵiringula,

adzayamba kuuzana kuti,

4“Ndi uyutu munthu uja tinkamuseka nkumunyozayu.

Tinali opusa!

Tinkayesa kuti moyo wake unali wamisala,

kutinso imfa yake inali yochititsa manyazi.

5Nanga adamuŵerengera bwanji

pamodzi ndi ana a Mulungu?

Adapezeka bwanji pakati pa anthu oyera mtima?

6Kwenikweni ndife amene tidasokera posiya njira yoona,

kuŵala kwa chilungamo sikudatiŵalire ife,

ndipo dzuŵa silidatitulukire.

7Tidayenda mosadzimana kanthu

m'njira ya kusamvera ndi ya chiwonongeko.

Tidayenda m'zipululu zopanda njira,

sitidadziŵe njira ya Ambuye.

8Nanga kunyada kwathu kudatipindulira chiyani?

Chuma chimene tinkachinyadira chidatipatsa chiyani?

9Zonsezi zidangozimirira

ngati mthunzi, ngati mphekesera.

10“Zonsezo zidangopita

ngati chombo chodutsa pa mafunde amphamvu,

chimene sichisiya mkwaso pamene chadutsa,

ndipo njira yake siwonekanso.

11Ndi ngatinso mbalame youluka m'mwamba,

osaonetsa chizindikiro cha njira yake,

koma tingoona mapiko ake akukupiza mu mpweya.

Ndi mphamvu zake imauluka mwaliŵiro,

koma sitiwonapo chizindikiro pamene yadutsa.

12Zilinso ngati muvi umene anthu auponya

pofuna kulasa kanthu,

mphepo imene waidula imabwerera msanga mwakale,

ndipo sitizindikira pamene yadutsa.

13Chimodzimodzinso ife, titabadwa chatsopano,

pompo tidaleka kukhala ndi moyo,

ndipo tinalibe nkanthu kabwino komwe koti tikasonyeze,

koma tidaonongekeratu ndi ntchito zathu zoipa.”

14Zoonadi chikhulupiriro cha munthu

wosamvera Mulungu chili ngati mungu

wouluzika ndi mphepo,

ngati thovu lopepuka lomwazika ndi namondwe.

Chili ngati utsi womwazika ndi mphepo,

chimazimirira msanga

monga momwe amaiŵalikira mlendo

wa tsiku limodzi lokha.

15Koma olungama ali ndi moyo wamuyaya.

Malipiro ao ali kwa Ambuye,

Wopambanazonse ndiye amaŵasamala.

16Nchifukwa chake adzalandira ulemerero waufumu

ndi nsangamutu yaulemu kuchokera kwa Ambuye,

pakuti Mulunguyo adzaŵateteza

ndi dzanja lake lamanja,

adzaŵachirikiza ndi mkono wake

ngati chishango.

17 Aef. 6.11-17 Iyeyo adzavala changu chake cholipsira

ngati zovala zankhondo,

zolengedwa zidzakhala ngati zida zake

zothyolera adani.

18Chilungamo chidzakhala ngati malaya ankhondo,

chiweruzo choona chidzakhala ngati chisoti chankhondo.

19Kuyera kwake kudzakhala

ngati chishango chosapambanika.

20Ukali wake udzakhala wakuthwa ngati lupanga.

Zolengedwa zonse za m'dziko lapansi

zidzamuthandiza kumenya nkhondo

yothyola adani ake openga.

21M'mitambo yamumlengalenga

yokhala ngati mauta okoka bwino,

mudzafumira mphezi zong'anima,

zimene zidzalasa adani ngati mivi yosaphonya.

22Ukali wa Mulunguwo udzaŵagwetsera matalala,

monga amachitira makina oponyera miyala.

Madzi am'nyanja adzaŵaopsa,

mitsinje idzaŵamiza mopanda chisoni.

23Mphepo yamkuntho idzaŵaukira,

idzaŵamwaza ngati kamvulumvulu.

Choncho kusaweruzika kudzasandutsa dziko lonse

kukhala chipululu,

machitidwe oipa adzagwetsa pansi

mipando ya mafumu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help