Mphu. 50 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Simoni mkulu wa ansembe

1Ndi Simoni, mwana wa Oniyasi, mkulu wa ansembe,

amene adakonza Nyumba ya Mulungu

pamene anali moyo,

naizinganso ndi malinga.

2Adakhazikitsa maziko a zipupa zazitali ziŵiri,

zolimbitsa khoma la Nyumba ya Mulungu ponse pozungulira.

3Pa nthaŵi yake anthu adakumba dziŵe la madzi,

dziŵe lake ngati nyanja kukula.

4Mtima wake unali pa kuteteza anthu ake kuti asaonongeke,

motero adalimbitsa mzinda kuti usagonje akauthira nkhondo.

5Ankaoneka waulemu kwambiri anthu akamzungulira

iye akamatuluka kuseri kwa chinsalu chochinga.

6Anali ngati nthanda yoŵala m'mitambo

kapena ngati mwezi pamene uli wathunthu.

7Anali ngati dzuŵa loŵala pa Nyumba ya Mulungu

Wopambanazonse,

kapena ngati kuŵala kwa utawaleza pa mitambo yonyezimira.

8Anali ngati maluŵa a pa nthaŵi ya phukira,

kapena ngati akakombo pafupi ndi kasupe wa madzi,

kapenanso ngati nthambi ya mtengo wa lubani

yonunkhira bwino pa dzinja.

9Anali ngati lubani wofuka m'chombo,

kapena ngati chikho chopangidwa ndi golide wosalala,

chimene adachikometsa ndi miyala yamtengowapatali.

10Anali ngati mtengo wa olivi wodzaza ndi zipatso

kapena ngati mkungudza wofika ku mitambo.

11Ankati akavala mkanjo wake wapamwambo,

nkukolekapo zokongoletsera zamakaka,

nkudzakwera ku guwa lansembe,

bwalo la Nyumba yopembedzeramo linkalemerera.

12Pamene ansembe ankampatsa zigawo za nsembe,

iye ataima pafupi ndi guwa,

abale ake ali kwete m'mbalimu,

anali ngati kamtengo ka mkungudza ka ku Lebanoni,

kokhala pakati pa kanjedza.

13Ana onse a Aroni, atavala zokongola,

ankaima pamaso pa gulu lonse la Aisraele,

ali ndi nsembe zopereka kwa Ambuye m'manja mwao.

14Atatha kuchita mwambo wapaguwa

ndi kupereka nsembe kwa Mulungu Wamphamvuzonse,

Wopambanazonse,

15ankatambalitsa dzanja nkugwira chikho,

nkuthira vinyo wa fungo lokoma patsinde pa guwa

ngati nsembe yopereka kwa Mulungu Wopambanazonse,

mfumu ya anthu onse.

16Tsono ana a Aroni ankafuula namaliza malipenga ao asiliva.

Ndipo ankachita phokoso lalikulu ngati

chikumbutso pamaso pa Ambuye.

17Pa nthaŵi yomweyo anthu onse pamodzi

ankadzigwetsa pansi moŵeramitsa mutu,

namapembedza Mulungu wao, Wamphamvuzonse,

Wopambanazonse.

18Ndipo gulu lanyimbo linkamutamanda ndi mau ao,

poimba nyimbo za maimbidwe okongola.

19Anthu ankapemba Ambuye Wopambanazonse

ndi kupemphera pamaso pa Mulungu Wachifundo

mpaka mwambo wa Ambuye utatha,

ndi kutsiriza dongosolo lake.

20 Num. 6.24-27 Tsono wansembe wamkulu ankatsika kuchokera ku guwa

nkukweza manja ake pa gulu lonse la Aisraele,

kuti aŵadalitse m'dzina la Ambuye.

21Ndiye anthu ankaŵerama pansi kachiŵiri

kuti alandire madalitso a Mulungu Wopambanazonse.

Pemphero lotamanda

22Tsopano tamandani Mulungu amene adalenga zonse,

amene amachita ntchito zodabwitsa kulikonse.

Ndiye amene amatilera kuyambira m'mimba mwa amai,

ndipo amatichitira chifundo.

23Atipatse chimwemwe chamumtima

ndipo masiku athu ano akhale amtendere

m'dziko la Israele mpaka muyaya.

24Ambuye azipitiriza kutichitira chifundo

ndipo atipulumutse pa nthaŵi yomwe ino.

Mitundu yoipa ya anthu

25Pali mitundu iŵiri ya anthu imene ndimaipidwa

nayo,

ndipo wachitatu si mtundu wa anthu konse.

26Amenewo ndi anthu okhala ku phiri la Seiri,

Afilisti ndi anthu opusa a ku Sekemu.

Nzeru za Yesu mwana wa Sira

27Ine Yesu, mwana wa Sira, mwana wa Eleazara wa

ku Yerusalemu,

ndalemba m'buku muno malangizo a luntha ndi a nzeru

ochokera mumtima mwanga.

28Ngwodala munthu amene amatanganidwa ndi kuphunzira

malangizo ameneŵa.

Amene amaŵasunga mu mtima, adzakhala wanzeru.

29Amene amasunga malangizo ameneŵa,

adzapambana pa zonse,

poti akuyenda m'kuŵala kwa Ambuye.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help