1 Eks. 25.22 Imvani, Inu Mbusa wa Israele,
Inu amene mumatsogolera anthu a Yosefe
ngati gulu la nkhosa.
Inu amene mumakhala pa akerubi
ngati pa mpando wanu wachifumu,
2dziwonetseni kwa mafuko a Efuremu
ndi Benjamini ndi Manase.
Onetsani mphamvu zanu,
ndipo mubwere kudzatipulumutsa.
3Inu Mulungu, tibwezereni mwakale,
mutiwonetse nkhope yanu yokondwa,
ndipo ife tidzapulumuka.
4Inu Chauta, Mulungu Wamphamvuzonse,
mudzakwiyira mapemphero a anthu anu mpaka liti?
5Mwaŵadyetsa chisoni ngati chakudya,
mwaŵapatsa misozi ngati chakumwa.
6Mwaŵasandutsa chinthu chonyozeka
kwa anzathu a mitundu ina,
ndipo adani athu akakhala pamodzi, amangotiseka.
7Inu Mulungu Wamphamvuzonse, tibwezereni mwakale,
mutiwonetse nkhope yoŵala, kuti ife tipulumuke.
8Mudatulutsa mpesa wanu Israele m'dziko la Ejipito.
Mudapirikitsa mitundu ina ya anthu kuti muubzale mpesawo.
9Mudaulimira munda mpesawo,
udamera mizu yozama, nudzaza m'dzikolo.
10Mapiri adaphimbidwa ndi mthunzi wake,
mikungudza yaikulu yomwe idaphimbidwa ndi nthambi zake.
11Nthambizo zidafika mpaka ku nyanja yaikulu yakuzambwe,
ndipo mphukira zake mpaka ku mtsinje waukulu wakuvuma.
12Nanga chifukwa chiyani mwagumula mpanda wake,
kuti opita m'njira azithyola nawo zipatso zake?
13Nguluŵe zam'nkhalango zimauwononga,
ndipo zonse zoyenda m'thengo zimaudya.
14Mutembenukirenso kwa ife, Inu Mulungu Wamphamvuzonse,
muyang'ane Inu okhala kumwamba, ndipo muwone.
Samalani mpesawo,
15mtengo woyambirira
umene Inu mudaubzala ndi dzanja lanu lamanja.
16Adani athu autentha, augwetsa pansi.
Ayang'aneni iwowo mokwiya ndi kuŵaononga.
17Koma ndi dzanja lanu
muteteze anthu amene mudaŵasankha,
anthu amene Inu nomwe mwaŵalimbikitsa
kuti akutumikireni.
18Tsono sitidzakusiyaninso,
tipatseni moyo,
ndipo tidzatama dzina lanu mopemba.
19Inu Chauta, Mulungu Wamphamvuzonse,
tibwezereni mwakale.
Mutiwonetse nkhope yoŵala,
kuti ife tipulumuke.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.