Mas. 21 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Davide athokoza chifukwa cha kugonjetsa adaniKwa Woimbitsa Nyimbo. Salmo la Davide.

1Mfumu ikusangalala

chifukwa mwaipatsa mphamvu, Inu Chauta,

ikukondwa kwambiri

chifukwa mwaipambanitsa ndinu.

2Mwaipatsa zimene mtima wake umakhumba,

simudaimane zimene pakamwa pake padapempha.

3Mumafika kwa mfumuyo ndi madalitso okoma kwambiri.

Mwaiveka chipewa chaufumu chagolide pamutu.

4Iyo idakupemphani moyo,

ndipo Inu mudaipatsa moyo wautali, wamuyaya.

5Ulemerero wake ndi waukulu

chifukwa mwaipambanitsa ndinu.

Mwaipatsa ufumu waukulu ndi waulemu.

6Zoonadi, mwaisandutsa yodala kopambana mpaka muyaya.

Mwaisangalatsa ndi chimwemwe, chifukwa muli nayo.

7Paja mfumuyo imakhulupirira Chauta,

ndipo siidzagwedezeka

chifukwa cha chikondi chosasinthika cha Wopambanazonse.

8Idzagonjetsa adani ake onse.

Dzanja lake lamphamvu lidzakantha onse odana nayo.

9Ikangotulukira, idzaŵaononga

monga m'mene ng'anjo yamoto imaonongera.

Chauta adzaŵatha phu, chifukwa cha kukwiya nawo,

ndipo iwo adzanyeka ndi moto kuchita kuti psiti.

10Mfumuyo idzaononga ana ao pa dziko lapansi,

zidzukulu zao zidzatha pakati pa anthu.

11Akafuna kuti aichite choipa ndi kuipweteka,

adzalephereratu,

12pakuti idzaŵapirikitsa

potendekera nkhope zao ndi mauta ake.

13Mutamandike, Inu Chauta,

chifukwa cha kupambana kwanu.

Tidzaimba ndi kuyamika mphamvu zanu zazikulu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help