Amo. 2 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chilango cha Amowabu

1 Yes. 15.1—16.14; 25.10-12; Yer. 48.1-47; Ezek. 25.8-11; Zef. 2.8-11 Zimene akunena Chauta ndi izi:

“Chifukwa Amowabu akunka nachimwirachimwira,

sindileka kuŵalanga.

Iwo adanyoza mafupa a mfumu ya ku Edomu

poŵatentha mpaka kuŵasandutsa phulusa.

2Nchifukwa chake Ineyo ndidzaponya moto ku Mowabu,

ndipo motowo udzapsereza malinga a ku Keriyoti.

Anthu a ku Mowabu adzafera pakati pa phokoso la nkhondo,

asilikali akufuula ndi kuliza malipenga.

3Ndidzaŵaphera wolamulira wao,

Ndidzaphanso nduna zake pamodzi naye.”

Akuterotu Chauta.

Chilango cha anthu a ku Yuda

4Zimene akunena Chauta ndi izi:

“Chifukwa anthu a ku Yuda

akunka nachimwirachimwira,

sindileka kuŵalanga.

Iwo anyoza malamulo a Ine Chauta,

ndipo sadatsate malangizo anga.

Milungu yabodza imene makolo ao

ankaipembedza yaŵasokeretsa.

5Nchifukwa chake Ineyo ndidzaponya moto ku Yuda,

ndipo motowo udzapsereza malinga a Yerusalemu.”

Chilango cha anthu a ku Israele

6Zimene akunena Chauta ndi izi:

“Chifukwa anthu a ku Israele

akunka nachimwirachimwira,

sindileka kuŵalanga.

Iwo amagulitsa anthu achilungamo ndi siliva,

amagulitsa anthu osauka ndi nsapato.

7Anthu osauka iwo amaŵadyera masuku pa mutu,

anthu ozunzika iwo safuna kuŵayang'ana.

Bambo ndi mwana amakagona ndi mdzakazi mmodzimmodzi,

mwakuti amanyoza dzina langa loyera.

8Anthuwo amagona pambali pa malo aliwonse opembedzerapo,

pa zovala zimene adalandira kwa osauka ngati chikole.

M'nyumba ya Mulungu amamweramo zakumwa

za anthu amene adaŵalipitsa pa mlandu.

9 Deut. 3.8-11 “Komabe ndine amene ndidaononga Aamori

pamene Aisraele ankafika,

ngakhale iwo aja anali ataliatali ngati mikungudza,

ngakhale anali amphamvu ngati mitengo ya thundu.

Ndidaŵaonongeratu zipatso zao m'mwamba

ndiponso mizu yao pansi.

10Inu Aisraele,

ndine ndidakutulutsani ku dziko la Ejipito.

Ndine ndidakutsogolerani m'chipululu zaka makumi anai,

kuti mukalande dziko la Aamori lija.

11 Num. 6.1-8 Ndipo ndine ndidasankha ena mwa ana anu

kuti akhale aneneri,

nkusankha ena mwa anyamata anu

kuti akhale Anaziri.

Kodi si choncho, inu anthu a ku Israele?”

Akuterotu Chauta.

12“Koma Inu mudaŵamwetsa vinyo Anaziri aja,

ndipo mudaŵalamula aneneriwo kuti, ‘Musalose.’

13“Mverani, ndidzakukanikizani pansi kwanuko,

ndipo mudzalira ngati ngolo

yodzaza ndi katundu wopitirira muyeso.

14Waliŵiro sadzatha kuthaŵa,

wanyonga sadzakhalanso ndi mphamvu.

Wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.

15Munthu wamauta sadzalimbika.

Wothamanga sadzapulumuka,

ndipo wokwera pa kavalo sadzapulumutsa moyo wake.

16Pa tsiku limenelo ngakhale wolimba mtima

pakati pa anthu a mphamvu,

adzathaŵa ali maliseche.”

Akuterotu Chauta.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help