Mphu. 39 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za munthu wophunzira

1Pali ntchito inanso yosiyana zedi,

ntchito ya munthu woika mtima pa kuphunzira za

Malamulo a Wamphamvuzonse.

Munthu ameneyo amafufuzafufuza nzeru za anthu akale

ndipo amaika mtima pa zimene aneneri adanena.

2Amasonkhanitsa nkhani za anthu otchuka

ndipo amayesetsa kulondola nzeru zozama

za mafanizo.

3Amasanthula matanthauzo obisika a miyambi

ndipo amatha kulongosola zinsinsi za nthano.

4Amagwira ntchito yotumikira akuluakulu

ndipo amapezeka pakati pa olamulira.

Amayenda ku maiko achilendo

kuti akafufuze za makhalidwe oipa ndi abwino a anthu.

5Amachita khama kuuka m'mamaŵa

kuthamangira kwa Ambuye, Mlengi wake,

ndipo amapemphera kwa Mulungu Wopambanazonse.

Amapemphera ndi mtima wonse ndi pakamwa pomwe

napepesa kuti amkhululukire machimo ake.

6Ambuye, Mulungu wamkulu, akafuna,

adzamdzaza nazo nzeru zodziŵira zinthu.

Pamenepo munthuyo adzalalika mau anzeru,

ndipo adzayamika Ambuye popemphera.

7Adzaongolera maganizo ake ndi nzeru zake pakuphunzira,

ndipo adzasinkhasinkha zachinsinsi

zimene adaphunzirazo.

8Pa zophunzitsa zake adzadziŵika

kuti ndi wanzeru,

adzanyadira Malamulo

a chipangano cha Ambuye.

9Ambiri adzamtamanda chifukwa cha nzeru zake,

ndipo sizidzaiŵalika.

Mbiri yake sidzafafanizika,

dzina lake lidzakhala lotchuka pa mibadwo yonse.

10Mitundu ya anthu idzakamba za nzeru zake,

ndipo mpingo udzamuyamika pa msonkhano.

11Akadzakhala ndi moyo nthaŵi yaitali,

adzakhala wotchuka koposa anthu chikwi chimodzi.

Akadzafa msanga,

mbiri yakeyo idzamkwanira.

Nyimbo yotamanda Mulungu

12Mumtima mwangamu muli zinanso zambiri zoti ndinene.

Ndili wodzaza monga m'mene umaonekera mwezi wathunthu.

13Ndimvereni, ana anga ouzika,

mukule monga duŵa lokongola lobzala m'mbali mwa mtsinje.

14Mwazani fungo lokoma ngati lubani,

phukani maluŵa ngati kakombo.

Mwazani fungo lokoma,

imbani nyimbo yotamanda.

Tamandani Ambuye chifukwa cha ntchito zao zonse.

15Lalikani za ukulu wa dzina la Ambuye,

muŵayamike ndi kuŵatamanda ndi nyimbo zapakamwa ndi azeze.

Muŵatamande ndi mau akuti,

16“Zonse zimene Ambuye adalenga nzabwino kwambiri.

Zonse zimene amalamula zimachitika pa nthaŵi yake.”

17Munthu wina asafunse kuti, “Kodi ichi nchiyani?

Nanga izo bwanji?”

Funso lililonse lili ndi nthaŵi yake.

Pamene Ambuye adalankhula, madzi adaundana,

mau ake adapanga maiŵe a madzi.

18Akalamula, chilichonse chimachitikadi momwe afunira,

palibe munthu amene angachepetse mphamvu zake zopulumutsira.

19Amaona zochita za anthu onse,

palibe choti nkubisira maso ake.

20Amakhala maso chiyambire cha nthaŵi mpaka muyaya,

palibe chinthu chodabwitsa pamaso pa Ambuye.

21Munthu wina asafunse kuti, “Kodi ichi nchiyani?

Nanga izo bwanji?”

Chinthu chilichonse chidalengedwa ndi cholinga chake.

22Madalitso ake ali ngati mtsinje wosefukira

umene umanyowetsa nthaka youma.

23Koma anthu akunja amaŵakwiyira,

monga adasandulitsa madzi abwino kuti akhale amchere.

24Kwa anthu oyera mtima njira za Mulungu nzolungama

koma kwa anthu ochimwa nzokhumudwitsa.

25Kuyambira pa chiyambi zinthu zabwino zidalengedwa

chifukwa cha anthu abwino,

zinthu zoipa zidalengedwa chifukwa cha anthu ochimwa.

26Zinthu zofunika kwambiri pa moyo wa munthu ndi izi:

madzi, moto, chitsulo, mchere,

ndiponso ufa, uchi, mkaka, vinyo, mafuta ndi zovala.

27Zonsezi nzabwino kwa anthu oopa Mulungu,

koma zimasanduka zoipa kwa anthu ochimwa.

28Pali mphepo zina zimene zidalengedwa kuti zizilanga anthu,

ndipo mkuntho wake umaŵasautsa.

Pa nthaŵi ya chiwonongeko zimaonetsa mphamvu zake,

zimapoza ukali wa amene adazilenga.

29Moto ndi matalala, njala ndi imfa,

zonsezi zidalengedwa kuti zikhale chilango.

30Zilombo, zinkhanira, mamba ndi lupanga

zimenezi nzolanga anthu osapembedza ndi kuŵaononga,

31Zonsezi zimakondwera kuchita zimene Mulungu amalamula.

Nzokonzeka kutumikira Ambuye pamene kufunikira,

ndipo nthaŵi yake ikakwana sizinyozera malamulo ake.

32Ndidazivomera zonsezi chiyambire,

ndipo nditaganizaganiza ndidalemba kuti,

33“Ntchito zonse za Ambuye nzabwino,

amapereka zonse zofunika pa nthaŵi yake.”

34Munthu wina asanene kuti,

“Ichi si chabwino ngati icho,”

chifukwa zinthu zonse zidzadziŵika kuti nzabwino

pa nthaŵi yake.

35Tiyeni tsopano, ndi mtima wanu wonse muimbe mokweza,

ndipo mutamande dzina la Ambuye.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help