1 Lun. 6.1-11 Muzikonda chilungamo,
inu olamulira dziko lino lapansi.
Muzikhala ndi maganizo olongosoka
pa kusinkhasinkha za Ambuye.
Muzifunafuna Iwowo ndi mtima woona.
2Pajatu amene sapenekera Ambuye, amaŵapezadi,
ndipo Ambuyewo amadziŵonetsa
kwa anthu oŵakhulupirira.
3Maganizo opotoka amalekanitsa anthu ndi Mulungu,
ndipo Iye amaŵachititsa manyazi
anthu opusa, ofuna kupeputsa mphamvu zake.
4Luntha sililoŵa mu mtima wa munthu wonyenga,
silikhala mwa munthu wogonjera machimo.
5Mzimu woyera, wophunzitsa anthu,
umaŵathaŵa anthu onyenga,
sukhalapo pamene pali maganizo opusa;
umakhumudwa ndi makhalidwe osalungama.
Mulungu amadziŵa maganizo athu6Luntha ndi mzimu wachifundo kwa anthu,
koma sililekerera munthu
wonyoza Mulungu mwachipongwe,
chifukwa Mulungu amadziŵa zam'kati zonse,
amafufuza za mumtima mwa munthu
ndi kumva zimene amalankhula.
7Ndithudi, mzimu wa Ambuye wadzaza
pa dziko lonse lapansi,
umagwirizira zinthu zonse pamodzi,
umadziŵa zonse zimene anthu amalankhula.
8Nchifukwa chake munthu wolankhula zoipa sangabisale,
chilungamo sichidzalephera kumutsutsa.
9Munthu wonyoza Mulungu adzazengedwa mlandu
pa zolinga zake,
nkhani yake idzafika mpaka kwa Ambuye
ndipo adzamutsutsa kuti ndi wopalamula ndithu.
10Khutu latcheru la Mulungu limamva zonse,
limamva ngakhale madandaulo ong'ung'udza.
11Tsono chenjerani
kuti musamangoŵiringula pachabe,
ndipo musakhale akazitape,
chifukwa ngakhale zonena kuseri
zimakhala ndi zotsatira zake,
ndipo wokamba zonama
amaononga moyo wamumtima.
Mulungu sadalenge imfa12Musadziitanire imfa
ndi mayendedwe anu oipa,
kapena kudzigwetsera chiwonongeko
ndi ntchito za manja anu.
13 Ezek. 18.32; 33.11; 2Es. 3.7; 2Pet. 3.9 Mulungu sadapange imfa,
sakondwera ndi imfa ya anthu amoyo.
14Iye adalenga zonse kuti zizikhalapo.
Zolengedwa zonse za m'dziko lapansi nzabwino,
zilibe ululu wopha anthu.
Imfa ilibe ulamuliro pansi pano,
15chifukwa chilungamo chidzakhalapo
mpaka muyaya.
16 Miy. 8.36; Yes. 28.15; Mphu. 14.12 Koma anthu osamvera Mulungu
amadziitanira imfa,
chifukwa cha ntchito zao ndi mau ao.
Amaisandutsa ngati bwenzi lao,
ndipo amailakalaka kwabasi.
Amachita nayo chipangano,
motero ayeneradi kukhala m'gulu lake.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.