Mas. 100 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nyimbo yotamanda pa nsembe yothokozeraSalmo loyamikira.

1Fuulani kwa Chauta ndi chimwemwe,

inu maiko onse.

2Tumikirani Chauta mosangalala.

Bwerani pamaso pake mukuimba mokondwa.

3Dziŵani kuti Chauta ndiye Mulungu.

Ndiye amene adapanga ife, ndipo ifeyo ndife ake.

Ndife anthu ake, nkhosa za busa lake.

4Loŵani pa zipata zake mukuthokoza,

pitani m'mabwalo a Nyumba yake mukutamanda.

Yamikani Chauta, lemekezani dzina lake!

5 1Mbi. 16.34; 2Mbi. 5.13; 7.3; Eza. 3.11; Mas. 106.1; 107.1; 118.1; 136.1; Yer. 33.11 Paja Iye ndi wabwino.

Chikondi chake nchamuyaya,

kukhulupirika kwake nkosatha.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help