Yes. 15 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mulungu adzaononga Mowabu

1 Yes. 25.10-12; Yer. 48.1-47; Ezek. 25.8-11; Amo. 2.1-3; Zef. 2.8-11 Nawu ulosi wonena za Mowabu:

Chifukwa chakuti mzinda wa Ari

waonongedwa usiku umodzi wokha,

dziko la Mowabu lagwa.

Chifukwa chakuti mzinda wa Kiri

waonongedwa usiku umodzi wokha,

dziko la Mowabu lagwa.

2Anthu a ku Diboni akukwera

ku nyumba ya milungu yao,

akukwera ku akachisi ao kukalira.

Anthu a ku Mowabu akulira mzinda

wa Nebo ndi wa Medeba.

Mutu uliwonse wametedwa mpala,

ndevu zonse zametedwa.

3M'miseu akuvala ziguduli,

pamadenga ndi m'mabwalo

aliyense akulira kwamphamvu,

misozi ili pupupu.

4Anthu a ku Hesiboni ndi ku Eleale

akulira mofuula.

Mau ao akumveka mpaka ku Yahazi.

Nchifukwa chake asilikali a ku Mowabu akulira mofuula,

ataya mtima.

5Inenso ndikulira Mowabu.

Anthu ake othaŵa nkhondo akuthaŵira

ku Zowari, ku Egilati-Selisiya.

Akupita nalira ku chikweza cha Luhiti,

akulira mosweka mtima pa mseu wopita ku Horonaimu.

6Ku mtsinje wa Nimurimu madzi adaphwa,

udzu udauma, msipu udafota,

palibenso chomera chobiriŵira.

7Nchifukwa chake anthu akuthaŵa

atanyamula chuma chao.

Afuna kuwoloka nacho Chigwembe cha Misondodzi.

8Kulira kwao kukumveka ku dziko lonse la Mowabu,

kukumveka kuchokera kumpoto ku Egilaimu

mpaka kumwera ku Beerelimu.

9Madzi a ku Diboni asakanizika ndi magazi,

komabe ndidzafikitsa zovuta zina zambiri pa Diboni.

Ndidzafikitsa mkango woti udzagwire

aliyense wopulumuka ku Mowabu,

ndiponso aliyense wotsalira m'dzikomo.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help