Yes. 66 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chauta agamula mlandu wa anthu a mitundu ina

1 Mt. 5.34; 23.22; Mt. 5.35 Ntc. 7.49, 50 Chauta akunena kuti,

“Thambo lam'mwamba ndiye mpando wanga waufumu,

dziko lapansi ndiye chopondapo mapazi anga.

Kodi ndi nyumba yotani

imene mungathe kundimangira inu?

Ndi malo otani amene inu mungandikonzere

kuti Ine ndizipumulirapo?

2Zinthu zonsezi ndidazilenga ndine,

tsono zonsezi nzanga,”

akutero Chauta.

“Anthu amene ndimakondwera nawo ndi aŵa:

odzichepetsa ndi olapa,

ondiwopa ndi omvera mau anga.

3“Koma pali ena amene amangochita zoŵakomera.

Kwa iwo nchimodzimodzi

kupereka ng'ombe yamphongo ngati nsembe

kapena kupha munthu,

kupha mwanawankhosa kuti aperekere nsembe

kapena kupha galu,

kupereka chopereka cha chakudya

kapena kupereka magazi a nkhumba,

kupereka lubani ku nsembe yachikumbutso

kapena kupembedza fano.

Anthu ameneŵa mtima wao umakondwera nazo zonyansa zao.

4Ine tsono ndidzaŵagwetsera chilango

ndipo ndidzaŵachititsa mantha,

chifukwa nditaŵaitana, palibe amene adandiyankha,

kapena kutchera khutu pamene ndinkalankhula.

Adachita zoipa pamaso panga,

adasankhula kuchita zimene zimandinyansa.”

5Imvani mau a Chauta,

inu amene mumanjenjemera akamalankhula.

Iye akuti, “Abale anu omwe amene amadana

nanu nakukanani chifukwa cha dzina langa,

amati, ‘Chauta alemekezeke,

kuti ife tiwone chimwemwe chanu.’

Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.

6“Imvani mfuu mu mzinda!

Imvani liwu m'Nyumba ya Mulungu,

liwu la Chauta amene akulanga adani ake.

7 Chiv. 12.5 “Mzinda wangawu uli ngati mai

amene akubadwitsa mwana

asanayambe kumva zoŵaŵa zake,

amene akubala mwana wamwamuna

kupweteka kusanayambike.

8Ndani adamvapo zoterezi?

Ndani adaziwonapo zoterezi?

Kodi dziko nkupangika tsiku limodzi?

Kodi mtundu wa anthu nkubadwa tsiku limodzi?

Koma Ziyoni adabala ana ake aamuna,

atangoyamba kuvutika kumene.

9Kodi ine ndidzafikitsa anthu anga

mpaka nthaŵi yobala,

koma osalola kuti abaledi?”

Akuterotu Chauta.

“Kodi Ine, amene ndili wobalitsa,

ndingatseke mimba nthaŵi imeneyo?”

Akuterotu Mulungu wako.

10“Kondwera nayeni Yerusalemu,

musangalale chifukwa cha iye,

inu nonse amene mumakonda mzinda umenewu.

Kondwera nayeni mwachimwemwe,

nonsenu amene mukumlira.

11Mudzalandira chitonthozo ndi

kukondwera nacho kwambiri.

Mudzagaŵana naye ulemerero wake

ndi kusangalala nawo.”

12Chauta akunena kuti,

“Ndidzakupatsa zabwino zochuluka

ngati mtsinje wa madzi.

Chuma cha mitundu ya anthu chidzafika kwa inu

ngati mtsinje wosefukira.

Mudzakhala ngati mwana woyamwa

amene mai wake wamnyamulira pambalipa,

kapena akumluluza pa maondo.

13Ndidzakusangalatsani ku Yerusalemu

monga momwe mai amasangalatsira mwana wake.

14Mudzasangalala poona zimenezi.

Zidzakulimbitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu.

Tsono mudzadziŵa kuti Ine Chauta

ndimathandiza amene amandimvera,

ndipo ndimakwiyira adani anga.”

15“Pajatu Chauta adzabwera ndi moto.

Ndipo magaleta ake adzafika ngati mkuntho.

Iye adzaonetsa poyera ukali wake,

ndipo adzalanga adani ake ndi malaŵi a moto.

16Adzalanga anthu onse a pa dziko lapansi

ndi moto ndi lupanga.

Alipo ambiri amene Chauta adzaŵapha.”

17Chauta akunena kuti, “Amene akuti akudzipatula ndi kudziyeretsa pamene akufuna kuchita miyambo yam'minda ija, ali ndi mtsogoleri wao yemwe, nkumadya nyama yankhumba, mbeŵa ndi zonyansa zina, onsewo adzafera limodzi,” akuterotu Chauta.

18“Ndikudziŵa ntchito zao ndi maganizo ao. Ndikubwera kudzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndi a zilankhulo zonse. Adzabweradi ndipo adzaona ulemerero wanga.

19“Ndidzaika chizindikiro pakati pao. Mwa iwowo padzakhala ena opulumukako amene ndidzaŵatuma kwa anthu a mitundu ina, monga a ku Tarisisi, a ku Puti ndi a ku Ludi, akatswiri a mauta, ndiponso ku Tubala, ku Yavani, ndi ku maiko akutali amene sadamvepo za mbiri yanga kapena kuwona ulemerero wanga. Iwowo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.

20Ndipo adzabwera nawo abale anu onse kuchokera kwa anthu a mitundu yonse, kuti akhale mphatso kwa Ine. Adzabwera nawo ku phiri langa loyera la Yerusalemu, abale anuwo ataŵakweza pa akavalo, abulu, ngamira ndiponso pa magaleta ndi ngolo. Adzabwera nawo monga momwe Aisraele amabwerera ndi zopereka za chakudya ku Nyumba ya Mulungu, atazitenga m'ziŵiya zotsukatsuka,

21ndipo ena mwa iwo ndidzaŵasandutsa ansembe ndi Alevi,” akutero Chauta.

22 Yes. 65.17; 2Pet. 3.13; Chiv. 21.1 “Monga momwe dziko lapansi latsopano

ndi dziko lakumwamba latsopano,

zimene ndidzapange,

zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga,

chonchonso zidzukulu zanu ndi dzina lanu

zidzakhala mpaka muyaya.

23Anthu a mitundu yonse adzabwera

kudzandipembedza ku Yerusalemu,

pa chikondwerero chilichonse cha pokhala mwezi,

ndi tsiku la Sabata lililonse,”

akutero Chauta.

24 Yud. 16.17; Mk. 9.48 “Akamachoka, adzaona mitembo ya anthu amene adandipandukira. Mphutsi zimene zidzaŵadya sizidzafa, ndipo moto umene udzaŵatentha sudzazima. Anthu a mitundu yonse poŵaona adzanyansidwa nawo.”

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help