Mas. 36 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za kuipa kwa munthuKwa Woimbitsa Nyimbo. Salmo la Davide, mtumiki wa Chauta.

1 Aro. 3.18 Uchimo umalankhula

mu mtima wa munthu wosamvera Mulungu.

Alibe mantha ndi Mulungu m'maganizo mwake.

2Amadzinyenga m'maganizo mwake,

kotero kuti tchimo lake sangathe kulizindikira

ndi kudana nalo.

3Mau a pakamwa pake ndi oipa ndi onyenga.

Sachita zanzeru kapena zabwino.

4Amaganiza zachiwembu akamagona usiku.

Amayenda pa njira imene siili yabwino,

sapewa zoipa.

Za ubwino wa Mulungu.

5Inu Chauta, chikondi chanu chosasinthika

chimafika mpaka kumwamba,

kukhulupirika kwanu kumafika mpaka ku mitambo.

6Kulungama kwanu kumaonekera ngati mapiri aatali,

kuweruza kwanu nkozama ngati nyanja yakuya,

Inu Chauta, mumasamalira anthu ndi nyama zomwe.

7Chikondi chanu chosasinthika ndi chamtengowapatali.

Nchifukwa chake anthu anu

amathaŵira m'munsi mwa mapiko anu.

8Mumaŵadyetsa zonona m'nyumba mwanu,

ndipo mumaŵamwetsa madzi a mu mtsinje wa madalitso anu.

9Kwa Inu kuli kasupe wamoyodi,

m'kuŵala kwanu ifenso timaona kuŵala.

10Musaleke kuŵakonda ndi chikondi chanu chosasinthika

anthu okudziŵani,

pitirizani kuŵachitira zokoma

anthu olungama mtima.

11Musalole kuti mapazi a anthu odzikuza andipondereze,

ndipo kuti manja a anthu oipa andipirikitse.

12Onani, ochita zoipa ali ngundangunda.

Inu mwaŵagwetsa pansi ndipo sangathe kudzuka.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help