Mas. 113 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kutamanda ubwino wa Chauta

1Tamandani Chauta!

Mtamandeni, inu atumiki ake,

tamandani dzina la Chauta.

2Yamikani Chauta

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3Dzina la Chauta litamandike

kuyambira ku matulukiro a dzuŵa

mpaka ku maloŵero ake.

4Chauta akulamulira anthu a mitundu yonse,

ulemerero wake ndi waukulu kuposa wa mlengalenga.

5Ndani angalingane ndi Chauta, Mulungu wathu,

amene akukhala kumwamba,

6wochita kuŵeramira pansi

poyang'ana mlengalenga ndi dziko lapansi.

7Amakweza munthu wosauka kuchokera ku fumbi,

ndipo amatulutsa ku dzala anthu osoŵa.

8Amaŵakhazika pamodzi ndi mafumu,

mafumu a anthu a Chauta.

9Amapatsa banja mkazi wosabala,

namsandutsa mai wosangalala wa ana.

Tamandani Chauta!

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help