Yer. 2 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mulungu ankasamala Aisraele

1Chauta adandiwuza kuti

2ndikalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu mau ake akuti,

“Ndikukumbukira m'mene munkakhulupirikira

pa unyamata wanu,

m'mene poyamba paja munkandikondera

monga amachitira mkwati wamkazi.

Mudanditsata m'chipululu,

m'dziko losabzalamo kanthu.

3Iwe Israele udaali wopatulika wa Chauta.

Udaali ngati chipatso chake choundukula.

Ndidaika zoŵaŵa ndi mavuto aakulu,

pa onse amene adakuzunza,

ndipo tsoka linkaŵagwera,” akutero Chauta.

4Inu zidzukulu za Yakobe, mabanja onse a Israele, mverani mau a Chauta.

5Iye akukufunsani kuti,

“Kodi makolo anu adandipeza ncholakwa chanji kuti andithaŵe?

Adatsata milungu yachabechabe,

iwonso nkusanduka achabechabe.

6Sadalabadeko za Ine Chauta,

ngakhale ndine amene ndidaŵatulutsa m'dziko la Aejipito,

ndi kuŵatsogolera m'chipululu,

m'dziko louma ndi lokumbikakumbika,

m'dziko lachilala ndi la mdima wandiweyani,

m'dziko limene munthu sadutsamo,

kumene sikukhala munthu konse.

7Ndidakufikitsani ku dziko lachonde

kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina.

Koma mutangoloŵa m'dzikolo, mudaliipitsa,

dziko limene ndidakupatsani mudalisandutsa lonyansa.

8Nawonso ansembe sadafunse kuti,

‘Chauta ali kuti?’

Akatswiri a malamulo sadandidziŵe.

Olamulira adandipandukira.

Aneneri ankalosa m'dzina la Baala,

ndipo ankatsata milungu yachabechabe.

Chauta aŵaimba mlandu anthu ake

9“Tsono ndidzakuimbanibe mlandu,”

akuterotu Chauta.

“Ndidzaimbanso mlandu zidzukulu zanu.

10Pitani chakuzambwe, ku chilumba cha Kitimu, mukaone,

tumani anthu chakuvuma, ku Kedara, akafufuze.

Mudzaona kuti zoterezi sizidachitikepo nkale lonse.

11Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse

umene udasinthapo milungu yake,

ngakhale kuti si milungu konse?

Komabe anthu anga asinthitsa Mulungu wao

waulemerero ndi milungu yachabechabe.

12Inu maiko akumwamba, dabwa nazoni zimenezi,

njenjemerani ndi mantha,

akuterotu Chauta.

13Anthu anga achita machimo aŵiri:

andisiya Ine kasupe wa madzi opatsa moyo,

adzikumbira okha zitsime,

zitsime zake zong'aluka, zosatha kusunga madzi.

Zotsatira za kusakhulupirika kwa Aisraele

14“Israele si kapolotu ai,

sadabadwire mu ukapolo.

Nanga chifukwa chiyani amuwononga chotere?

15Anthu a mitundu ina ambangulira

ndi kumuwopsa ngati mikango.

Dziko lake alisandutsa chipululu.

Mizinda yake adaiwononga, idasanduka mabwinja.

16Aejipito a ku Memfisi ndi a ku Tapanesi

akuphwanyani mitu.

17Zimenezi zakuwonekerani

chifukwa mudasiya Chauta, Mulungu wanu,

pamene Iye adakuikani pa njira yabwino.

18Nanga tsopano mudzapindulanji mukadzapita ku Ejipito,

kukamwa madzi a m'Nailo?

Mudzapeza phindu lanji mukadzapita ku Asiriya

kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?

19Mudzalangidwa ndi machimo anu omwe:

poti mwandikana, ndidzakuimbani mlandu.

Muganizire bwino za kuipa kwake kwa kundisiya Ine,

Chauta, Mulungu wanu.

Mulingalire kuŵaŵa kwake kwa kukhala osandiwopa,”

akuterotu Ambuye, Chauta Wamphamvuzonse.

Aisraele akana kupembedza Chauta

20“Kuyambira masiku amakedzana inu mudathyola goli lanu

ndi kudula nsinga zanu.

Mudati, ‘Sitidzakutumikirani!’

Ndithu inu mwakhala ngati mkazi wadama,

mukupembedza milungu ina pochita zadama

pa phiri lililonse

ndiponso pansi pa mtengo wogudira uliwonse.

21Komabe ndidaakuwoka iwe Israele

ngati mtengo wa mphesa wosankhidwa,

udaali mpesa wabwino kwambiri.

Nanga wasanduka bwanji mpesa wachabechabe,

wonga wakutchire?

22Ngakhale usambire soda,

ngakhale usambire sopo wambiri,

kuthimbirira kwa tchimo lako

kumaonekabe pamaso panga,”

akuterotu Ambuye Chauta.

23“Uneneranji kuti, ‘Ine sindidadziipitse,

sindidatsate Baala?’

Kumbukira m'mene udachimwira m'chigwamo,

zindikira zimene wachita.

Wakhala ngati ngamira yaikazi,

yothamanga uku ndi uku.

24Wakhala ngati mbidzi yaikazi yozoloŵera m'chipululu,

yonka nipunika pa nthaŵi yake yachisika.

Kodi angailetse chilakolako chakecho ndani?

Mphongo iliyonse yoikhumba sidzavutika,

idzaipeza pa nthaŵi yakeyo.

25Iwe Israele, lekatu, nsapato zingakuthere ku phazi,

kukhosi kwako kungaume ndi ludzu potsatira milungu ina.

Koma iwe ukuti,

‘Ai toto, sindingathe kuchitira mwina,

ndimakonda milungu yachilendoyi,

sindingaleke kuitsata.’

Israele ayenera kulangidwa

26“Banja la Israele lidzachita manyazi,

monga momwe mbala imachitira manyazi akaigwira.

Aisraele, mafumu ao ndi akalonga ao,

ansembe ao ndi aneneri ao,

onsewo adzachita manyazi.

27Amauza mtengo kuti ‘Iwe ndiwe bambo wathu,’

amauza mwala kuti ‘Iwe ndiwe amene udatibala.’

Koma Ine amandifulatira,

m'malo motembenukira kwa Ine.

Tsono akakhala pa mavuto amati,

‘Dzambatukani, mutithandize.’

28Nanga milungu yanu ili kuti,

milungu ija mudadzipangira ija?

Idzambatuketu, ngati ingathe kukupulumutsani

pa nthaŵi yanu ya mavuto.

Inu anthu a ku Yuda, milungu yanu ndi yambiri,

kuchuluka kwake monga momwe iliri mizinda yanu.”

29Chauta akuti,

“Kodi mukundiimbiranji mlandu?

Nonsenu mwandipandukira.

30Ndidalanga ana anu popanda phindu,

sadaphunzirepo nkanthu komwe.

Monga mkango wolusa mudapha aneneri anu ndi lupanga.”

31Inu anthu amakono, imvani mau a Chauta.

“Kodi ndakhala ngati chipululu kwa Israele,

kapena ngati dziko la mdima wandiweyani?

Chifukwa chiyani tsono anthu anga akunena kuti,

‘Ndife mfulu,

sitidzabweranso kwa Inu?’

32Kodi namwali amaiŵala zokongoletsera zake,

kapena mkwati kuiŵala zovala zake zaukwati?

Komabe anthu anga andiiŵala Ine masiku osaŵerengeka.

33“Mumadziŵa bwino njira zopezera zibwenzi zam'seri.

Ngakhale akazi oipa kwambiri omwe mumaŵaphunzitsa ndinu.

34Zovala zanu zili psu

ndi magazi a anthu osauka osachimwa.

Anthuwo simudaŵapeze nathyola nyumba.

Komabe, ngakhale zinthu zili choncho,

35inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa,

mkwiyo wa Chauta wapola tsopano!’

Ine ndidzakuimbanibe mlandu

chifukwa chonena kuti simudachimwe.

36Bwanji mukudzipeputsa nokha

posinthasintha njira zanu!

Ejipito adzakugwiritsani mwala

monga muja adakuchititsirani manyazi Aasiriya.

37Mudzatuluka kumeneko

aliyense atagwirira manja ku mutu.

Ine Chauta ndidaŵakana amene inu mumagonerapo,

ndipo anthuwo sadzakuthandizani mpang'ono pomwe.”

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help