1Izi ndi zimene Obadiya adaona m'masomphenya.
Naŵa mau a Ambuye Chauta onena za Aedomu.
Chauta adatuma wamthenga wake
kwa anthu a mitundu yonse,
ndipo tidamva mau ake, adati,
“Konzekani, tiyeni tikamenyane nkhondo ndi Aedomu.”
2Chauta akuuza Aedomu kuti,
“Ndithu ndidzakutsitsani kotheratu,
anthu a mitundu yonse adzakunyozani kwambiri.
3Mwanyengedwa ndi mtima wanu wonyada.
Likulu lanu lili pakati pa matanthwe,
mumakhala pa mapiri aatali.
Mumanena kuti, ‘Ndani angatitsitse pansi?’
4Komatu ngakhale muuluke pamwamba ngati chiwombankhanga,
ngakhale mumange chisa chanu pakati pa nyenyezi,
ndidzakutsitsanibe pansi.”
Akutero Chauta.
5“Akuba akabwera usiku,
amangotengako zimene akufuna.
Okolola akamathyola zipatso,
amasiyako zina.
Koma inuyo adani anu akupululani kotheratu.
6Onani m'mene alisakazira dziko la Esau,
ndi m'mene achifunkhira chuma chake chonse.
7Ogwirizana nanu akunyengani,
akupirikitsani m'dziko mwanu.
Okuthandizani pa nkhondo akugonjetsani.
Abwenzi anu apamtima akutcherani msampha,
mwathedwa nzeru tsopano.”
8Chauta akuti,
“Nthaŵi imeneyo ndidzaononga anzeru onse a ku Edomu,
ndidzathetsa kuchenjera konse kwa zidzukulu za Esau.
9Ngwazi za ku Temani zidzachita mantha,
ankhondo onse adzaphedwa ku mapiri a Esau.
Zolakwa za Aedomu10“Aedomu inu, chifukwa cha zankhanza
zimene mudachita abale anu, zidzukulu za Yakobe,
adzakuchititsani manyazi ndi kukuwonongani mpaka muyaya.
11Munkangoonerera pamene adani ankaŵalanda chuma chao,
munkachita ngati kuvomerezana nawo,
amene ankaloŵa pa zipata za Yerusalemu,
namagaŵana chumacho.
12Inu simukadayenera kuŵanyodola abale anu Ayuda
chifukwa cha tsoka lao.
Simukadayenera kukondwerera kuwonongeka kwao.
Simukadayenera kuŵaseka
pamene iwo anali m'mavuto.
13Pa tsiku lao la tsoka
simukadayenera kuloŵa mu mzinda wa anthu anga.
Pa tsiku lao la tsoka
simukadayenera kuŵanyodola.
Pa tsiku lao la tsoka
simukadayenera kulanda chuma chao.
14 Yes. 34.5-17; 63.1-6; Yer. 49.7-22; Ezek. 25.12-14; 35.1-15; Amo. 1.11, 12; Mal. 1.2-5 Simukadayenera kudikira pa mphambano za miseu
kuti mugwire anthu othaŵa.
Pa tsiku lao la tsoka
simukadayenera kupereka anthu ao otsala kwa adani.
Tsiku la Chauta15“Posachedwapa lifika tsiku la Chauta
pamene Iye adzaweruza mitundu yonse ya anthu.
Aedomu inu, adzakuchitani zomwe mudaŵachita ena.
Zimene mudachitazo zidzakubwererani.
16Anthu anga adamwa chikho cha zoŵaŵa
pa phiri langa loyera,
koma mitundu ina ya anthu
idzamwa chikho cha zoŵaŵa kopitirira.
Idzachita kugugudiza chikhocho
kenaka nkuzimirira pomwepo.
Israele adzapambana17“Koma pa phiri la Ziyoni padzakhala ena opulumuka,
ndipo phirilo lidzakhala loyera.
Pamenepo fuko la Yakobe lidzalandira choloŵa chakechake.
18Fuko la Yakobe lidzakhala ngati moto,
fuko la Yosefe lidzakhala ngati malaŵi a moto,
fuko la Esau lidzakhala ngati ziputu.
Adzaŵatentha ndi kuŵapsereza,
ndipo sipadzapulumuka munthu aliyense.”
Akutero Chauta.
19Ayuda akumwera adzalandira phiri la Esau,
akuzambwe adzalandira dziko la Afilisti.
Akumpoto adzalandira dziko la Efuremu
ndi likulu lake Samariya,
ndipo Abenjamini adzalandira dziko lakuvuma la Giliyadi.
20Aisraele amene anali ku ukapolo
adzalandira dziko la Kanani
mpaka kumpoto ku Zarefati.
A ku Yerusalemu amene anali ku ukapolo ku Sefaradi
adzalandira mizinda yakumwera ku Negebu.
21Ngwazi zochokera ku Yerusalemu
zidzagonjetsa ndi kumalamulira dziko la Edomu
ndipo ufumu wonse udzakhala wa Chauta.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.