1Tsopano konzekani m'magulu ankhondo,
inu a ku Yerusalemu.
Atizinga ndi zithando zankhondo,
akuthira nkhondo likulu la Israele.
Za Mfumu yochokera ku Betelehemu2 Mt. 2.6; Yoh. 7.42 Chauta akuti,
“Koma iwe Betelehemu wa ku Efurata,
inde ndiwe wamng'ono pakati pa mafuko a Yuda,
komabe mwa iwe ndidzatulutsa munthu
amene adzakhala wolamulira Israele.
Iyeyo chiyambi chake nchakalekale,
cha masiku amakedzana.”
3Nchifukwa chake Mulungu adzasiya Israele
mpaka pa nthaŵi yoti achire
mkazi amene adzabale mwana.
Pamenepo, otsala a mtundu wake
adzabwereranso kwa Aisraele anzao.
4Iye adzalimbikira, ndipo adzaŵeta nkhosa zake
mwa mphamvu za Chauta
ndi ulemerero wa dzina la Chauta,
Mulungu wake.
Ndipo iwo adzakhala mu mtendere,
poti ukulu wake udzakhazikika pa dziko lonse lapansi.
5Ndiye amene adzakhazikitse mtendere.
Aisraele apulumuka kenaka nkulangidwaAasiriya akadzaloŵa m'dziko mwathu
ndi kuyamba kutithira nkhondo,
tidzaŵatumira atsogoleri ankhondo asanu ndi aŵiri
kapena akalonga asanu ndi atatu.
6 Gen. 10.8-11 Iwowo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga,
dziko la Nimirodi adzalilamulira mwankhondo.
Adzatipulumutsa kwa Aasiriya,
iwowo akadzakaloŵa m'dziko mwathu,
kudzatithira nkhondo.
7Onse otsalira a Yakobe adzakhala dalitso
pakati pa mitundu yambiri ya anthu
ngati mame ochoka kwa Chauta.
Adzakhala ngati mvula yowaza pa udzu,
imene sichita kulamulidwa ndi anthu,
siidikira lamulo la munthu.
8Onse otsalira a Yakobe
adzakhala temberero
pakati pa mitundu ya anthu,
ngati mkango pakati pa nyama zam'nkhalango.
Adzakhala ngati mwana wa mkango,
pakati pa gulu la nkhosa,
amene amati akadzaziloŵerera,
amazimbwandira ndi kuzikadzula.
Ndipo sipakhala wozipulumutsa.
9Inu Aisraele, mudzapambana adani anu,
ndipo adani anu onsewo adzaonongeka.
10Komabe Chauta akuuza Aisraele kuti,
“Pa tsiku limenelo ndidzaononga akavalo anu onse,
ndipo ndidzaphwasula magaleta anu.
11Ndidzaononga mizinda ya m'dziko mwanu
ndi kugwetseratu malinga anu.
12Ndidzasakaza masenga anu onse,
ndipo pakati panu sipadzakhalanso oombeza.
13Ndidzaononga mafano anu onse
pamodzi ndi miyala yoimika
yopembedzerapo m'dziko mwanu.
Simudzazigwadiranso zinthuzo
zimene mudapanga ndi manja anu.
14Ndidzagwetsa mafano anu a Asera m'dziko mwanu,
ndipo ndidzaononga mizinda yake.
15Mwaukali ndi mokwiya
ndidzalanga mitundu yonse ya anthu
imene sidandimvere.”
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.