Mphu. 25 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za mwamuna wabwino ndi mwamuna woipa

1Pali zinthu zitatu zimene zimasangalatsa

mtima wanga,

zimenenso zimakondweretsa Mulungu ndi anthu onse.

Zinthu zake ndi izi: chiyanjano pakati pa abale,

chibwenzi pakati pa anthu oyandikana,

ndipo mwamuna ndi mkazi okhalitsana bwino.

2Pali anthu a mitundu itatu amene ndimadana nawo

amene moyo wao umandinyansa kwambiri.

Anthu ake ndi aŵa:

munthu wosauka amene ali wonyada,

munthu wolemera amene ali wonama,

ndipo nkhalamba yokonda zigololo imene ilibe nzeru.

3Ngati sudapeze kanthu ukali mwana,

kodi ungapate kanthu bwanji utakalamba?

4Kuganiza mwanzeru kumaŵakhala bwino anthu aimvi,

ndipo kulangiza ena bwino kumazikhala bwino nkhalamba.

5Nzeru zimaŵakhaladi bwino anthu okalamba

ndipo khalidwe lakumvetsa ndi lauphungu

limaŵayenerera akuluakulu olemekezeka.

6Ulemerero wa munthu wokalamba wagona pa

kudziŵa zinthu zambiri,

ndipo chimene amanyadira nkuwopa Ambuye.

7Pali zinthu zisanu ndi zinai zondisangalatsa mtima,

palinso china chakhumi chimene ndichita kunena:

munthu wonyadira ana ake,

munthu wotha kuwona kugwa kwa adani ake iye akali moyo.

8Ngwodala mwamuna amene ali ndi mkazi wanzeru,

ngwodala mlimi amene saphatikiza ng'ombe ndi

bulu polima ndi pulao,

ngwodala munthu amene sanachimwepo polankhula,

ngwodalanso munthu amene sadagwirire ntchito

munthu woluluka koposa iye.

9Ngwodala munthu amene ali ndi nzeru zabwino,

munthu woti akalankhula anzake amatchera khutu.

10Ngwamkuludi munthu amene wapeza nzeru,

komabe munthu woopa Ambuye palibe amene angampose.

11Kuwopa Ambuye kumapambana zonse.

Kodi munthu woopa Ambuye tingamfanizire ndi yani?

12Kuwopa Ambuye ndiye chiyambi cha kuŵakonda Ambuyewo,

ndipo chikhulupiriro ndiye chiyambi cha

kuphathikana nawo.

Za mkazi woipa

13Bala lililonse chabwino, koma osati bala lokhala mu mtima.

Njiru iliyonse chabwino, koma osati njiru ya munthu wamkazi.

14Vuto lililonse chabwino, koma osati vuto lochokera

kwa odana nawe.

Kulipsira kulikonse chabwino, koma osati kulipsira kwa mdani.

15Palibe ululu woopsa kupambana wa njoka,

ndipo palibe mkwiyo woopsa kupambana mkwiyo wa mdani.

16Ndi bwino kukhala pamodzi ndi mkango kapena chinjoka,

kupambana kukhala pamodzi ndi mkazi woipa.

17Mkazi akakwiya,

maonekedwe ake amasinthika,

nkhope yake imaoneka ngati

ya chimbalangondo chaukali.

18Mwamuna wake amapita kukadya nawo kwa anzake,

sangaleke kudandaula kwambiri.

19Choipa china chilichonse si kanthu,

kuyerekeza ndi njira ya mkazi.

Tsoka la anthu ochimwa ligwere mkaziyo.

20Monga momwe imavutikira nkhalamba pokwera

phiri lamchenga,

ndi m'menenso amavutikira mwamuna wofatsa

ndi mkazi wolongolola.

21Usatengeke naye mtima mkazi wokongola,

ndipo usakhumbire mkazi wachuma.

22Ngati ndi mkazi amene akupeza ndalama zofunikira pa banja,

zotsatira zake ndi mkwiyo, kulongolola ndiponso manyazi aakulu.

23Manyazi, nkhope yotsika, ndi kupwetekedwa mtima

ndizo zimene amabweretsa mkazi wanjiru.

Manja aulesi ndi maondo olobodoka, ndizo zimene

amabweretsa mkazi wosasangalatsa mwamuna wake.

24Tchimo lidayamba ndi munthu wamkazi.

Ngati tonsefe timafa, nchifukwa cha iyeyo.

25Usalole madzi kutayikira pa mng'alu.

Usalolenso mkazi woipa kumalankhula mwamwano.

26Ngati sachita zinthu

monga m'mene ukulamulira iweyo, usiyane naye.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help