Mas. 101 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Lonjezo la mfumuSalmo la Davide.

1Ndidzaimba nyimbo

zotamanda kukhulupirika ndi kulungama.

Ndidzakuimbirani Inu Chauta.

2Ndidzatsata njira yopanda cholakwa.

Nanga mudzabwera liti kwa ine?

Ndidzakhala ndi mtima wangwiro m'nyumba mwanga.

3Sindidzaika maso anga

pa chinthu chilichonse chachabechabe.

Ndimadana ndi zochita za anthu okusiyani,

sizindikomera konse.

4Ndidzakhala kutali ndi anthu a mtima woipa,

sindidzalola choipa chilichonse kuloŵa mwa ine.

5Munthu wosinjirira mnzake kuseri ndidzamcheteketsa.

Wooneka wonyada ndi wodzikuza sindidzamulekerera.

6Koma anthu okhulupirika am'dziko,

ndidzaŵayang'ana moŵakomera mtima,

ndipo adzakhala ndi ine.

Oyenda m'njira yopanda cholakwa adzanditumikira.

7Palibe munthu wochita zonyenga

amene adzakhale m'nyumba mwanga.

Palibe munthu wolankhula zabodza

amene adzakhale pafupi ndi ine.

8Tsiku ndi tsiku ndidzaononga oipa onse am'dziko.

Onse ochita zoipa ndidzaŵachotsa mu mzinda wa Chauta.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help