Nyi. 8 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1Ha! Achikhala unali mlongo wanga,

woyamwa bere limodzi ndi ine!

Ndikadakumana nawe panjira,

bwenzi ntakumpsompsona,

ndipo wina aliyense sakadandinyoza.

2Ndikadakutenga

nkukuloŵetsa m'nyumba ya amai anga,

m'chipinda cha amene adandibala.

Ndikadakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe,

ndi madzi a makangaza.

3Ine ndikadatsamira dzanja lako lamanzere,

iwe nkundikumbatira ndi dzanja lamanja.

4Inu akazi a ku Yerusalemu,

ndithu ndakupembani,

chikondichi musachigwedeze kapena kuchiwutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

Nyimbo Yachisanu ndi chimodzi

Akazi

5Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo,

atatsamira wokondedwa wake?

Mkazi

Ndidakudzutsa patsinde pa mtengo wa apulosi uja.

Pamenepo mpamene amai ako adachirira pokubala iweyo.

6Umatirire mtima wako

kuti musaloŵe winanso koma ine ndekha,

ndipo sudzakumbatira winanso koma ine ndekha.

Paja chikondi nchamphamvu ngati imfa,

nsanje njaliwuma ngati manda.

Chikondi chimachita kuti laŵilaŵi

ngati malaŵi a moto,

ndipo nchotentha koopsa.

7Ngakhale madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,

ngakhale madzi a chigumula sangachikokolole.

Ngakhale munthu atapereka chuma chonse cha m'nyumba

chifukwa chofuna kugula chikondi,

adzangonyozeka nazo kotheratu.

Alongo a Mkazi

8Tili naye ife mlongo wathu wamng'ono,

alibe ndi maŵere omwe.

Tidzamchitira chiyani mlongo wathu

pa tsiku limene adzamfunsire mbeta?

9Iye akakhala ngati khoma,

tidzammangira nsanja yasiliva.

Koma akakhala ngati chitseko,

tidzamchinga ndi matabwa amkungudza.

Mkazi

10Ine ndili ngati khoma,

ndipo maŵere anga ali ngati nsanja zake.

Tsono m'maso mwa wokondedwa wanga

ndili ngati wodzetsa mtendere.

Mwamuna

11Solomoni anali ndi munda wamphesa ku Baala-Hamoni.

Mundawo adaubwereka alimi.

Aliyense mwa iwo ankayenera kupereka

ndalama zasiliva chikwi chimodzi kuti azilimamo.

12Koma munda wanga wamphesa ndi wangawanga,

ndiponso wa ine ndekha.

Iwe Solomoni, khala nazo ndalama chikwi chimodzi zija,

khala nawonso alimi ako mazana aŵiri aja.

13Iwe amene umakhala m'munda

anzanga akumvetsera kuti amve liwu lako.

Tandilola kuti ndilimve.

Mkazi

14Fulumiratu wokondedwa wanga,

khala ngati mphoyo

kapena ngati mwanawambaŵala wothamanga m'mapiri,

m'mene mumamera mbeu zokometsera chakudya.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help