Mas. 120 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1Ndimalirira Chauta m'mavuto anga

kuti andiyankhe.

2Ndimati, “Pulumutseni, Inu Chauta,

kwa anthu onama ndi kwa anthu onyenga.”

3Mulungu adzakuchitani chiyani, anthu onyenganu?

Kodi adzakupatsani chilango cha mtundu wanji?

4Adzakuzunzani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo,

pamodzi ndi makala amoto a mtengo wa tsanya.

5Ndili ndi tsoka lalikulu,

chifukwa ndimakhala pakati pa anthu

onga mbuli za ku Meseki ndi Kedara.

6Ndakhala nthaŵi yaitali

pakati pa anthu odana ndi mtendere.

7Ine ndimafuna mtendere,

koma ndikalankhula za mtendere, iwo amafuna nkhondo.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help