Mla. 3 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Zonse zimachitika pa nthaŵi yake

1Pansi pano chinthu chilichonse chili ndi nyengo yake

ndi nthaŵi yake yomwe adaika Mulungu:

2pali nthaŵi yobadwa

ndi nthaŵi yomwalira,

pali nthaŵi yobzala

ndi nthaŵi yozula zobzalazo.

3Pali nthaŵi yakupha

ndi nthaŵi yochiritsa,

nthaŵi yogwetsa

ndi nthaŵi yomanga.

4Pali nthaŵi yomva chisoni

ndi nthaŵi yosangalala,

nthaŵi yolira maliro

ndi nthaŵi yovina.

5Pali nthaŵi yokhala malo amodzi

ndi nthaŵi yotalikirana,

nthaŵi yokumbatirana

ndi nthaŵi yoleka zokumbatiranazo.

6Pali nthaŵi yofunafuna

ndi nthaŵi yotaya,

nthaŵi yosunga

ndi nthaŵi yomwaza.

7Pali nthaŵi yong'amba

ndi nthaŵi yosoka,

nthaŵi yokhala chete

ndi nthaŵi yolankhula.

8Pali nthaŵi yokondana

ndi nthaŵi yodana,

nthaŵi ya nkhondo

ndi nthaŵi ya mtendere.

9Kodi wantchito amapeza phindu lanji pa ntchito yake yolemetsa?

10Ndaziwona ntchito zimene Mulungu adapatsa anthu kuti azizigwira.

11Adapanga chinthu chilichonse kuti chikhale chabwino pa nthaŵi yake. M'mitima mwa anthu Mulungu adaikanso nzeru zotanthauzira zochitika za pa mibadwo ndi mibadwo. Komabe anthuwo sangathe kuzitulukira ntchito zonse za Mulungu kuyambira pa chiyambi mpaka pomalizira.

12Ndikudziŵa kuti kwa anthu palibe chabwino china choposa kukhala osangalala ndi kumadzikondweretsa nthaŵi yonse ya moyo wao.

13Ndi mphatso ya Mulungu kwa anthu kuti azidya, azimwa ndi kumakondwera ntchito zao zolemetsa.

14Ndikudziŵa kuti zimene Mulungu amazichita zimakhazikika mpaka muyaya. Palibe zimene zingathe kuwonjezedwa kapena kuchotsedwapo pa zimenezo. Mulungu adazipanga motero, kuti choncho anthu azimumvera.

15Zimene zilipo tsopano zidaaliponso kale. Zimene zidzakhalepo kutsogolo, zidaaliponso kale. Mulungu amabwezanso zakale zimene zidapita kuti zichitikenso.

Pa dziko lapansi palibe chilungamo

16China chimene ndidachiwona pansi pano ndi ichi: Koyenera kukhala chiweruzo chabwino, komwekonso kumapezeka kuipa mtima. Koyenera kukhala chilungamo, komwekonso kumapezeka zoipa.

17Ndiye ine ndidayamba kulingalira kuti, “Mulungu adzaŵaweruza onse, abwino ndi oipa omwe, pakuti adaika nthaŵi yochitikira chinthu chilichonse ndiponso ntchito iliyonse.”

18Kunena za anthu, ndinkalingaliranso kuti, “Mulungu amaŵayesa ndi cholinga choti aŵaonetse kuti iwowo sasiyana konse ndi nyama.

19Zimene zimachitikira anthu, zomwezonso zimachitikira nyama. Monga chinacho chimafa, chinacho chimafanso. Zonsezo zimapuma mpweya umodzimodzi, munthu saposa nyama. Zonsezi nzopandapake.

20Zonse zimapita kumodzimodzi. Zonsezo nzochokera ku dothi, ndipo zimabwerera kudothi komweko.

21Kodi ndani angatsimikize kuti mzimu wa munthu ndiwo umakwera kumwamba, koma mpweya wa nyama umatsikira kunsi kwa nthaka?

22Choncho ndidaona kuti palibe chinthu chabwino kuposa kuti munthu azikondwerera ntchito yake, pakuti chake chenicheni nchimenechi. Ndani angathe kudziŵa chimene chidzamchitikire iye atafa?”

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help