Yow. 2 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chilango cha Chauta

1Lizani lipenga ku Ziyoni.

Fuulani mochenjeza pa phiri langa loyera.

Onse okhala m'dziko anjenjemere,

pakuti tsiku la Chauta likufika, layandikira.

2Ndi tsiku lamdima ndi lachisoni,

tsiku lamitambo ndi la mdima wandiweyani.

Gulu la ankhondo amphamvu ochuluka

langoti bii ngati mdima wokuta mapiri.

Gulu lotere silinaonekepo nkale lonse,

ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.

3Kutsogolo kwake moto ukupsereza,

kumbuyo kwake malaŵi a moto akutentha zinthu.

Iwo asanafike, dziko linali ngati munda wa Edeni,

koma atachoka, lidasanduka chipululu!

Palibe kanthu kotsalapo.

4 Chiv. 9.7-9 Maonekedwe ake ali ngati a akavalo,

liŵiro lake ngati la akavalo ankhondo.

5Akulumpha pamwamba pa mapiri

ndi phokoso longa la magaleta.

Akumveka ngati malaŵi a moto otentha ziputu,

ngati gulu lamphamvu lankhondo

litakonzekera kumenya nkhondo.

6Anthu a mitundu ina amachita mantha akaŵaona,

nkhope zonse zimatumbuluka.

7Akududuka ngati ankhondo.

Akukwera malinga ngati asilikali.

Aliyense akuyenda pa mzere,

osasempha njira yake.

8Sakukankhanakankhana,

aliyense akuyenda molunjika.

Akupyola pakati pa zida zankhondo, osaŵaimitsa.

9Akuulumphira mzindawo,

akukwera pamwamba pa malinga.

Akuloŵa m'nyumba,

akuloŵera pa windo ngati mbala.

10 Chiv. 8.12 Dziko lapansi likugwedezeka

pamene iwo akuyandikira.

Mlengalenga ukunjenjemera.

Dzuŵa ndi mwezi zikuchita mdima,

ndipo nyenyezi zikuleka kuŵala.

11 Chiv. 6.17 Chauta akumveketsa liwu lake

kutsogolo kwa gulu lake lankhondo.

Gulu lake lankhondolo ndi lalikulu kwambiri.

Wochitadi zimene Chauta akulamula, ngwamphamvu.

Tsiku la Chauta ndi lalikulu ndi loopsa.

Ndani angathe kupirira tsikulo?

Mulungu aitana anthu kuti abwerere

12Koma Chauta akunena kuti,

“Ngakhale tsopano bwererani kwa Ine

ndi mtima wanu wonse,

mukusala zakudya, mukukhetsa misozi

ndi kulira mwachisoni.

13Ng'ambani mitima yanu, osati zovala zanu chabe.”

Bwererani kwa Chauta, Mulungu wanu,

poti Iye ngwokoma mtima ndi wachifundo,

wosakwiya msanga ndi wa chikondi chosasinthika.

Nthaŵi zonse ndi wokonzeka kukhululuka.

14Mwina mwake adzasintha mtima ndi kuleka,

ndipo adzatisiyira madalitso.

Madalitsowo adzakhala a chopereka cha chakudya

ndi chakumwa

zopereka kwa Chauta,

Mulungu wanu.

15Lizani lipenga ku Ziyoni.

Lengezani mwambo wa kusala zakudya.

Muitanitse msonkhano waukulu.

16Sonkhanitsani anthu pamodzi,

muŵauze kuti adziyeretse.

Sonkhanitsani akuluakulu,

sonkhanitsani ana,

sonkhanitsani ndi oyamwa omwe.

Lamulani kuti nawonso akwati achoke

m'chipinda mwao, abwere.

17 1Am. 7.36-38 Ansembe, amene ali atumiki a Chauta,

azilira pakati pa guwa lansembe ndi khonde.

Azinena kuti,

“Inu Chauta, achitireni chifundo anthu anu.

Musalole kuti ena aŵanyoze

anthu anu osankhidwa.

Anthu achikunja asaŵaseke

pomafunsana kuti,

‘Ha, ali kuti Mulungu waoyo?’ ”

Mulungu akhululukira Israele

18Apo chikondi cha Chauta chidayaka

ngati moto chifukwa cha dziko lake,

ndipo adaŵachitira chifundo anthu ake.

19Chauta adaŵayankha anthu ake kuti,

“Ndikutumizirani tirigu, vinyo ndi mafuta,

ndipo mudzakhuta ndithu.

Sindidzalolanso kuti akunja akunyozeni.

20Ndidzachotsa adani akumpoto

kuti akhale kutali ndi inu,

ndipo ndidzaŵapirikitsira ku dziko

louma ndi lachipululu.

Akutsogolo ndidzaŵathamangitsira

ku nyanja yakuvuma,

akumbuyo ndidzaŵathamangitsira

ku nyanja yakuzambwe.

Tsono mitembo yao idzatulutsa

chivundi ndi fungo lonunkha.

Zoonadi Chauta adachita zazikulu.

21“Iwe dziko, usachite mantha.

Kondwa ndipo usangalale,

pakuti Chauta mwini wake adachita zazikulu.

22Inu nyama zakuthengo, musaope,

pakuti msipu wakuchipululu akuphukira.

Mitengo ikubala zipatso.

Mkuyu ndi mpesa zikubereka kwamphamvu.

23“Inu anthu a ku Ziyoni, kondwani ndi

kusangalala chifukwa cha zimene Chauta,

Mulungu wanu, wakuchitirani.

Wakukomerani mtima pokupatsani mvula mofulumira.

Wakupatsani mvula yochuluka,

kumayambiriro ndi kumathero,

monga pa masiku amekedzana.

24“Pa malo opunthira padzadzaza tirigu.

Mopondera mphesa mudzasefukira vinyo watsopano,

mafutanso adzachuluka.

25Motero ndidzakubwezerani zonse

zimene zidaonongedwa ndi dzombe,

mandowa, mphutsi ndi ziwala.

Limenelitu ndiye gulu lankhondo lija

limene ndidatuma kudzakukanthani.

26“Mudzadya zambiri ndi kukhuta,

ndipo mudzatamanda dzina la Chauta,

Mulungu wanu,

amene wakuchitirani zodabwitsa.

Choncho anthu anga sadzaŵanyozanso ai.

27Mudzadziŵa kuti Ine ndili naye Israele,

ndipo kuti Ine ndekha, osati wina,

ndine Chauta, Mulungu wanu.

Anthu anga sadzaŵanyozanso ai.

Za kubwera kwa Tsiku la Chauta

28“Patapita nthaŵi, tsiku lidzafika

pamene ndidzatsitsa mzimu wanga

pa mtundu uliwonse wa anthu.

Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzalosa.

Nkhalamba zanu zidzalota maloto,

ndipo achinyamata anu adzaona zinthu m'masomphenya.

29Masiku amenewo, ndidzatsitsa mzimu wanga

ngakhale pa akapolo ndi pa adzakazi omwe.

30“Mu mlengalenga ndi pa dziko lapansi ndidzaonetsa zodabwitsa izi: magazi, moto ndi utsi watoloo.

31Mt. 24.29; Mk. 13.24, 25; Lk. 21.25; Chiv. 6.12, 13 Dzuŵa lidzasanduka mdima, ndipo mwezi udzasanduka magazi, tsiku lalikulu ndi loopsa la Chauta lisanafike.

32Ntc. 2.17-21

Aro. 10.13 Ndipo aliyense amene adzatama dzina la Chauta mopemba, adzapulumuka. Monga Iye adanenera, kudzakhala ena opulumuka ku phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo mwa otsalawo padzapezeka ena amene Chauta adzaŵaitana.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help