Yob. 28 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1“Ndithudi, ulipo mgodi wa siliva,

alipo malo oyengerapo golide.

2Chitsulo amachikumba pansi,

mkuŵa amachita kuusungunula ku miyala yamkuŵa.

3Anthu amaloŵa mu mdima atatenga nyale

namafunafuna miyalayo mpaka ku malire a mgodiwo,

akuyenda mu mdima wandiweyani.

4Amakumba njira zapansi mumgodimo,

kutali ndi kumene kumakhala anthu,

mpaka kuiŵalika ndi anthu onka nayenda,

amakhala ali lende pansipo, namazunguzika uku ndi uku.

5Nthaka imatulutsa chakudya,

koma kunsi kwake kumachita ngati kofwantchuka ndi moto.

6Miyala yamumgodimo ndi ya safiro,

mulinso fumbi la golide.

7“Njira ya mu mgodi imeneyi,

palibe mbalame yodya zinzake imene imaidziŵa,

kamtema yemwe sanaiwone.

8Zilombo zolusa sizinapondemo m'njiramo.

Mkango sunadzeremo m'menemo.

9“Anthu amaphwanya matanthwe olimba,

amagadabula mapiri kuyambira m'tsinde.

10Amasema mipita m'matanthwemo,

ndipo amatulutsamo miyala ya mtengo wapatali.

11Amaletsa mitsinje yapansipo kuti isayende,

motero amaonetsa poyera zinthu zobisika.

12 Mphu. 1.6; Bar. 3.15 “Koma nzeru zingapezeke kuti?

Luntha lingapezeke kuti?

13 Bar. 3.29-31 Anthu sadziŵa kufunika kwake kwa nzeruzo,

ndipo sizipezeka pa dziko lino lapansi.

14Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno,’

nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ai.’

15Nzeru sangazipate ndi golide,

mtengo wake sangauyerekeze ndi siliva wambiri.

16Ngakhale golide wokoma kwambiri

wa ku Ofiri sangafike pa mtengo wa nzeruzo,

miyala ya onikisi kapena ya safiro

nayonso singafikepo.

17Golide ndi mwala wagalasi

sizingakwanire kuti agulire nzeru.

Nzeru sangazisinthanitse ndi

zokometsera za golide weniweni.

18Mtengo wake wa nzeru ndi woposa

miyala ya korali ndi krisitala,

umapambananso ndi miyala ya rubi yomwe.

Mtengo wake wa nzeru umapambana ndi ngale zomwe.

19Miyala ya topazi ya ku Etiopiya

sungaiyerekeze ndi nzeru,

ngakhale golide wabwino kwambiri sangafikepo pa nzeru.

20“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti?

Nkuti kumene tingapeze luntha?

21Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse,

ndi obisikanso kwa mbalame zamumlengalenga.

22Ngakhale malo a chiwonongeko

ndiponso imfa zimangoti,

‘Tidangomva mphekesera chabe ya zimenezo.’

23 Bar. 3.35-37 “Mulungu yekha ndiye amadziŵa

njira yake yopita kumeneko,

amadziŵa kumene nzeruzo zimakhala.

24Paja Iye amayang'ana mpaka

ku mathero a dziko lapansi,

amaona zonse zimene zili kunsi kwa thambo.

25Pamene Iye adapatsa mphepo mphamvu zake,

nayesa kuzama kwa nyanja,

26pamene adakhazika lamulo loti mvula izigwa,

nakonza njira za ching'aning'ani cha bingu,

27 Mphu. 1.9, 19 pamenepo mpamene adaona nzeruzo naziyesa mtengo wake,

ndipo adazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.

28 Mas. 111.10; Miy. 1.7; 9.10 Choncho adauza munthu kuti,

‘Kuwopa Ambuye ndiye nzeru zimenezo,

kuthaŵa zoipa ndiye luntha limenelo.’ ”

Yobe

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help