Mas. 32 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za kuulula machimo ndiponso za chikhululukiroNdakatulo ya Davide.

1 Aro. 4.7, 8 Ngwodala amene zolakwa zake zakhululukidwa,

amene machimo ake afafanizidwa.

2Ngwodala amene Chauta samuŵerengera mlandu wake,

amene mumtima mwake mulibe zonyenga.

3Pamene ndinali ndisanaulule tchimo langa,

thupi langa linali lofooka,

chifukwa cha kubuula tsiku lonse.

4Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu lidandipsinja,

motero nyonga zanga zidatha,

monga amafotera masamba ndi dzuŵa lachilimwe.

5Koma ndidavomera tchimo langa kwa Inu,

sindidabise kuipa kwanga.

Ndidati, “Ndidzaulula machimo anga kwa Chauta,”

pomwepo Inu mudakhululukiradi

mlandu wa machimo anga.

6Nchifukwa chake munthu aliyense wosamala za Inu

apemphere kwa Inu.

Akadzafika mavuto, akadzafika madzi a chigumula,

zonsezo sizidzamufika.

7Inu ndinu kobisalira kwanga.

Inu mumanditchinjiriza nthaŵi yamavuto.

Nchifukwa chake ndimaimba nyimbo

zotamanda chipulumutso chanu.

8Chauta akuti,

“Ndidzakudziŵitsa ndi kukuphunzitsa njira

imene uyenera kuyendamo.

Ndidzakulangiza ndi kukuyang'anira.

9“Musakhale opanda nzeru ngati kavalo kapena bulu

amene ayenera kumuwongolera

ndi chitsulo cham'kamwa ndi chapamutu,

chifukwa ukapanda kutero, nyamazo sizidzakumvera.”

10Anthu oipa amapeza zoŵaŵa zambiri,

koma munthu wokhulupirira Chauta

amazingidwa ndi chikondi chosasinthika.

11Sangalalani ndi kukondwa

inu nonse okonda Mulungu,

chifukwa cha zimene Chautayo adakuchitirani.

Inu anthu ake onse, fuulani ndi chimwemwe.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help