1Inu Aisraele, bwererani kwa Chauta,
Mulungu wanu,
pakuti mwagwa chifukwa cha machimo anu,
2Bwererani kwa Chauta, ndipo mumpemphe kuti,
“Mutikhululukire machimo athu onse.
Mumvere pempho lathu
ndipo tidzakuyamikani ndi mau otamanda.
3Aasiriya sadzatipulumutsa,
akavalo ankhondo sadzatiteteza.
Chimene tidapanga ndi manja athu
sitidzachitchulanso kuti, ‘Mulungu wathu,’
pakuti ndinu amene mumachitira chifundo amasiye.”
Chauta alonjeza moyo watsopano kwa Aisraele4Chauta akuti,
“Ndidzachiza matenda ao a kusakhulupirika.
Ndidzaŵakonda kwambiri,
pakuti ndaleka kuŵakwiyira.
5Ndidzatsitsimutsa Israele ngati mame.
Adzachita maluŵa ngati kakombo,
adzazika mizu ngati mtengo wa ku Lebanoni.
6Ziphukira zake zidzatambasukira kutali,
adzakhala wokongola ngati mtengo wa olivi,
adzakhala wonunkhira ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
7Aisraele adzapezanso chitetezo mwa Ine.
Adzakolola tirigu wambiri,
adzachuluka ngati mphesa.
Adzakhala otchuka ngati vinyo wa ku Lebanoni.
8Kodi Aefuremu adzachita nawonso chiyani mafano?
Ndine amene ndimamva pemphero lao ndi kuŵasamala.
Ndili ngati mkungudza wogudira nthaŵi zonse,
ndine amene ndimaŵapatsa zipatso.”
Mau omariza9Amene ali wanzeru amvetse zimenezi.
Amene ali womvetsa, azisunge.
Pakuti njira za Chauta nzolungama,
ndipo olungama amayendamo,
koma ochimwa amakhumudwamo.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.