1Inu Ambuye, mutichitire chifundo,
Inu Mulungu mwini zonse, mutiyang'ane ife.
2Muwopseze anthu onse a mitundu ina.
3Musamule dzanja lanu ndi kulanga mitundu yachilendo,
kuti onsewo adziŵe mphamvu zanu.
4Monga mudaŵaonetsera kuti ndinu oyera pa
zochita zanu pakati pa ife,
momwemonso mutiwonetse ukulu wanu pa zochita
zanu pakati pa iwowo.
5Aphunzire monga tidaphunzirira ife,
kuti palibe Mulungu wina koma Inu nokha Ambuye.
6Onetsani zizindikiro zatsopano ndi kuchita zozizwitsa zinanso,
muwonetse ulemerero wa dzanja lanu ndi mkono wanu wakumanja.
7Mudzutse mkwiyo wanu, mugwetse ukali wanu,
onongani amaliwongo ndi kuthyoleratu adani.
8Mulifulumize tsiku lake,
ndi kukumbukira nthaŵi yake yosankhidwa.
Anthu azisimba za ntchito zanu zodabwitsa.
9Ukali wa mkwiyo wanu uwononge anthu otsala,
adani a anthu anu atheretu.
10Phwanyani mitu ya mafumu a adani athu
amene amati, “Ife pano! Pali yaninso?”
11Sonkhanitsani mafuko onse a Yakobe,
muŵapatsenso dziko lao, monga mudaachitira kale.
12Inu Ambuye, muŵachitire chifundo anthu
otchedwa dzina lanuŵa,
Israele amene mudamutchula mwana wanu wachisamba.
13Muchitire chifundo mzinda
m'mene muli Nyumba yopembedzeramo Inu,
Yerusalemu, mzinda wopumulirako Inuyo.
14Mudzaze Ziyoni ndi nyimbo zambiri zokutamandani,
Nyumba yanu muidzaze ndi ulemerero wanu.
15Achitireni umboni anthu amene mudaŵalenga pa chiyambi,
muchitedi zimene aneneri adalankhula m'dzina lanu.
16Apatseni mphotho anthu okukhulupirirani,
ndipo aneneri anu apezeke kuti ngokhulupirika.
17Inu Ambuye, mverani pemphero la atumiki anu,
potsata zimene mudalonjeza pamene Aroni
adadalitsa anthu anu.
Apo anthu onse a dziko lapansi adzadziŵadi
kuti Inu ndinu Ambuye, Mulungu wamuyaya.
Za kusankhula18M'mimba mumaloŵa zakudya zosiyanasiyana,
koma chakudya china chimapambana chinzake.
19Monga lilime limazindikira
mitundu yosiyanasiyana ya nyama,
chonchonso munthu wanzeru
amatha kuzindikira mabodza.
20Munthu wa nzeru zopotoka amadzetsa mavuto,
nkofunika munthu wodziŵa zambiri kuti ambwezere
munthu wotere.
Za kusankha mkazi21Munthu wamkazi amavomera ukwati
mwamuna aliyense,
koma ana aakazi ena ali bwino
koposa anzao.
22Kukongola kwa munthu wamkazi kumasangalatsa
omuyang'ana,
amuna safuna chinanso kuposa pamenepo.
23Ngati mkazi ngwolankhula mofatsa ndi modzichepetsa,
mwamuna wake ngwamwai kupambana amuna ena onse.
24Munthu akatenga mkazi, ndiye kuti wagwira pakulu,
ali ndi mthandizi womuyenera ndiponso nsanamira
yoyedzamirako.
25Kumene kulibe mpanda, mbala zimabako.
Munthu amene alibe mkazi, ntchito nkuyendayenda
ndi kudandaula.
26Ndanitu angakhulupirire mbala yomangoyendayenda
m'mizinda yosiyanasiyana?
Chimodzimodzi ndani angakhulupirire munthu wopanda kwao,
womangogona kulikonse kumene kwamdera?
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.