Lun. 11 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Eks. 15.22—17.16 Luntha lidapambanitsa Aisraele pa ntchito zao

kudzera mwa mneneri woyera mtima.

2Adayenda m'chipululu chopanda anthu,

namanga mahema ao

pamalo pamene sipadapite anthu.

3Adalimbikira pamaso pa amaliwongo ao,

nkuŵapambana adani aowo pa nkhondo.

4Atamva ludzu adakupemphani,

Inu nkuŵapatsa madzi

otumphuka m'thanthwe lolimba zedi,

mudapha ludzu lao potulutsa madzi

m'thanthwe lagwaa.

Mulungu alanga Aejipito

5Zimene zidasautsa adani ao ngati chilango,

zidasanduka za phindu kwa eniakewo

pa nthaŵi ya mavuto ao.

6M'malo mwa kasupe wa madzi

oyenda nthaŵi zonse,

adani ao adapeza madzi oonongeka,

ataipa ndi magazi,

7ngati chilango chifukwa cha lamulo lao lija

loti ana aphedwe.

Koma anthu anu mudaŵapatsa madzi ochuluka,

pamene iwo sankayembekezako.

8Zimenezo zidachitika mutaŵamvetsa ludzu,

kuti adziŵe m'mene mudalangira adani ao.

9Pamene munkaŵayesa pakuŵalanga mwachifundo,

iwo adaphunzira m'mene mudazunzira mwaukali

anthu osamvera.

10Pajatu mudaŵayesa ndi kuŵapatsa phunziro,

monga m'mene bambo amachenjezera ana ake.

Koma ena aja mudaŵasautsa,

monga momwe mfumu yankhanza imalangira osamvera.

11Adani ao ankapezabe mavuto,

ngakhale anthu anu atakhala pafupi kapena kutali.

12Chisoni chidaŵagwira moŵirikiza,

ndipo ankabuula pokumbukira

zimene zidaŵagwera kale.

13Pakumva kuti zilango zao

zidathandiza anthu anu olungama,

adaniwo adazindikira kuti

zimenezi adaachita ndi Ambuye.

14Munthu uja amene iwowo adaamutaya kale lija

kenaka nkumuchotsa monyoza,

pambuyo pake adazizwa naye kwakukulu,

chifukwa ludzu lao

lidaapambana kwambiri la anthu olungama.

15 Eks. 8.1-24; 10.12-15 Chifukwa cha maganizo ao opusa ndi oipa,

amene adaŵasokeretsa mpaka kuŵapembedzetsa njoka

ndi nyama zonyansa,

mudaŵalanga pakuŵatumizira unyinji

wa zolengedwa zinanso zopanda nzeru.

16Choncho mudaŵaphunzitsa

kuti choipa chitsata mwini.

17Dzanja lanu lamphamvuzonse,

limene lidapanga zinthu zonse

kuchokera ku chinthu chosakonzeka,

likadatha kuŵatumizira zilombo zochuluka

ndi mikango yaukali.

18Likadathanso kuŵatumizira

zilombo zina zosadziŵika,

zolengedwa chatsopano,

za ukali woopsa,

zopuma mpweya wamoto,

zotulutsa utsi wonunkha m'kamwa,

kapena zoponya zing'aning'ani zoopsa

kuchokera m'maso mwake.

19Zolusazo zikadatha kuwonongadi anthuwo,

komanso ngakhale kungoziwona kokha

kukadatha kupha anthuwo ndi mantha.

20Ngakhale popanda zimenezo,

anthuwo akadatha kufa,

Inu mutangoŵauzira mpweya kamodzi kokha,

poŵalondola ndi chilungamo chanu

ndi kuŵamwaza ndi mpweya wanu wamphamvu.

Koma Inu mudafuna kukonza zonse molongosoka,

mutaziŵerenga ndi kuziyesa pa sikelo.

Mulungu ndi wamphamvu ndiponso wachifundo

21Mphamvu zanu mutha kuzigwiritsa ntchito

nthaŵi iliyonse.

Ndani angalimbikire kulimbana ndi dzanja lanu?

22Pamaso panu dziko lonse lapansi lili

ngati kamchenga kopendeketsa sikelo,

ngati dontho la mame am'mamaŵa logwa pa nthaka.

23Komabe chifukwa mungathe kuchita zinthu zonse,

mumaŵachitira chifundo anthu onse.

Mumapsinya maso dala

kuti musaone machimo a anthu,

kuti apeze mpata wotembenukira mtima.

24Mumakonda zolengedwa zonse,

palibe ncholengedwa chimodzi chomwe

chimene chingakunyanseni.

Mukadadana ndi kanthu,

bwenzi mutaleka kukalenga.

25Kanthu kalikonse kakadakhala moyo bwanji,

mukadapanda kukafuna?

Kakadakhalitsa bwanji,

Inu mukadapanda kukasunga?

26Koma zinthu zonse mumazichitira chifundo,

chifukwa zonse nzanu, Inu Ambuye,

amene mumakonda kwambiri chamoyo chilichonse.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help