Yes. 21 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za kugwa kwa Babiloni

1Nawu ulosi wonena za chipululu

cha m'mbali mwa nyanja.

Tsoka lidzafika kuchokera ku dziko lochititsa mantha

monga m'mene kamvulumvulu amakunthira

kuchokera ku chipululu.

2Ndaona zinthu zoopsa m'masomphenya:

wofunkha akufunkha,

woononga akuwononga.

Ankhondo a ku Elamu, yambani nkhondo!

Ankhondo a ku Mediya, zingani mzindawo.

Ine Chauta ndidzathetsa mavuto onse

amene adadza ndi Babiloni.

3Nchifukwa chake zimene ndidazimva ndi

kuziwona m'masomphenya zija zandichititsa mantha,

ndipo ndamva nazo ululu ngati mkazi amene akuchira.

Ndikuvutika nazo zimene ndilikumva.

Ndikuda nazo nkhaŵa zimene ndikuwonazi.

4Mtima wanga ukugunda,

ndipo ndikunjenjemera ndi mantha.

Ndakhala ndikulakalaka chisisira,

koma chisisiracho chandibweretsera zoopsa.

5Iwo akukonza tebulo ndi kuyala mphasa,

alikudya, alikumwa.

Mwadzidzidzi alikumva mau akuti,

Dzukani inu ankhondo,

pakani mafuta zishango zanu!

6Pakuti Ambuye andiwuza kuti,

“Pita, kaike mlonda

kuti azinena zimene akuwona.

7Akamaona anthu aŵiriaŵiri okwera pa akavalo,

okwera pa abulu ndi okwera pa ngamira,

mlondayo akhale tcheru, tcherutu zedi!”

8Apo mlondayo adafuula kuti,

“Ambuye, usana wonse ndimakhala pa nsanja,

usiku wonse ndimakhala pa malo anga olondera.

9 Chiv. 14.8; 18.2 Ndidangoona kukubwera anthu okwera pa akavalo,

akuyenda aŵiriaŵiri.

Mmodzi mwa iwo adati,

‘Ii, wagwa, wagwatu uku Babiloni!

Mafano onse a milungu yake

aphwanyikira pansi.’ ”

10Ndiye abale anga Aisraele,

inu opunthidwa ndi opetedwa ngati tirigu,

tsopano ndakuuzani uthenga

umene ndamva kwa Chauta Wamphamvuzonse,

Mulungu wa Israele.

Ulosi wonena za Edomu

11Nawu ulosi wonena za Edomu:

Wina akundilankhula mofuula

kuchokera ku Edomu, akuti,

“Iwe mlonda, usikuwu utha liti?

Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”

12Mlonda akuti, “Kulikucha, koma kudanso.

Ukafuna kufunsanso, ubwerenso udzafunse.”

Ulosi wonena za Arabiya

13Nawu ulosi wonena za Arabiya:

Inu anthu a ku Dedani oyenda pa gulu,

amene usiku mumagona m'malunje a ku Arabiya,

14muŵapatse madzi anthu aludzu kuti amwe.

Inu anthu a ku Tema,

muŵapatse chakudya anthu othaŵa nkhondo.

15Pakuti akuthaŵa malupanga,

malupanga osololasolola,

mauta okokakoka,

ndiponso nkhondo yoopsa.

16Ambuye adandiwuza kuti, “Chatsala chaka chimodzi, potsata m'mene amaŵerengera munthu waganyu, ndipo ulemu wonse wa anthu a ku Kedara udzatheratu.

17Mwa anthu onse amphamvu a ku Kedara okoka mauta, opulumuka adzakhala oŵerengeka.” Chauta, Mulungu wa Israele, watero.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help