Mphu. 3 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Za Udindo wa ana kwa makolo

1Ana inu, mundimvere ine bambo wanu.

Mukafuna kupulumuka,

muchite zimene ndikuuzeni.

2Ambuye adapatsa bambo ulemu woposa ana ake,

adatsimikiza mphamvu za mai pa ana ake.

3Amene amalemekeza atate ake,

amapepesa Mulungu

chifukwa cha machimo ake.

4Amene amalemekeza amai ake,

amachita ngati kudzikundikira chuma.

5Amene amalemekeza atate ake,

ana ake adzamsangalatsa,

ndipo akamapemphera,

mapemphero ake adzamveka.

6Amene amalemekeza atate ake,

adzakhala ndi moyo wautali.

Amene amamvera Ambuye,

amasangalatsa amai ake.

7Amene amaopa Ambuye,

amalemekeza atate ake,

amagwirira ntchito makolo ake

ngati mtumiki wao.

8 Eks. 20.12 Mwana wanga,

uzilemekeza atate ako ndi mau apakamwa

ndiponso ndi ntchito zako,

kuti madalitso ao akhale pa iwe.

9Pajatu madalitso a bambo

amalimbitsa mabanja a ana ake,

koma matemberero a mai

amazula maziko a mabanjawo.

10Usadzikweze pakuchititsa manyazi bambo wako.

Manyazi a bambo wako angakupatse bwanji ulemu?

11Munthu amapeza ulemu

chifukwa cholemekeza atate ake.

Ndipo kusalemekeza amai

nchinthu chochititsa ana manyazi.

12Mwana wanga, usamale bambo wako atakalamba,

usamuvute konse pa moyo wake wonse.

13Ngakhale nzeru zake zikuyamba kutha,

iwe uzimuwonetsa ndithu chifundo.

Usamnyoze chifukwa chongoti uli ndi moyo wolimba.

14Chifundo chochitira bambo wako sichidzaiŵalika,

adzachiŵerengera ngati cholipirira machimo ako.

15Pamene udzagwe m'mavuto

Mulungu adzakukumbukira,

ndipo machimo ako

adzasungunuka ngati chisanu pa dzuŵa.

16Amene sasamala bambo wake,

ali ngati munthu wonyoza Mulungu mwachipongwe.

Amene amakwiyitsa mai wake,

Ambuye amamtemberera.

Za kudzichepetsa

17Mwana wanga,

ukhale wodekha pa zonse zimene umachita,

ndipo anthu okomera Ambuye adzakukonda.

18 Afi. 2.3 Ngati ndiwe wotchuka kwambiri, udzichepetse,

ukatero udzapeza kuyanja pamaso pa Ambuye.

19Pali anthu ambiri otchuka ndi amphamvu,

koma Ambuye amaulula zinsinsi zao

kwa anthu odzichepetsa.

20Pajatu mphamvu za Ambuye nzazikulu,

amalemekezedwa ndi anthu odzichepetsa.

21Usayese kumvetsa zinthu

zimene zili zapatali kwa iwe,

kapena kufufuza zinthu

zimene zili zopitirira nzeru zako.

22 Deut. 29.29 Uzilingalira kwambiri

za ntchito imene walandira,

zimene zili zobisika kwa iwe

ulibe nazo ntchito.

23Usatanganidwe ndi zinthu

zopitirira nzeru zako,

ngakhale zimene adakuphunzitsa

nzopitirira nzeru za anthu.

24Ambiri adasokera

chifukwa cholingalira zinthu zapatali,

ndipo zopeka zao zonama

zidasokeretsa maganizo ao.

Za kunyada

25Ngati ulibe maso,

sungathe kupenya.

Ngati ndiwe mbuli,

usadziwonetse ngati wanzeru.

26Munthu wokanika adzatha moipa.

Munthu woseŵera ndi zoopsa,

adzataya moyo wake.

27Mtima wokanika umadzitengera mavuto ambiri,

munthu wochimwa amanka nachimwirachimwira.

28Tsoka likagwera wonyada,

palibe mankhwala,

pakuti kuipa kumakhala kutazika mizu mwa iye.

29Munthu wochenjera amalingalira bwino fanizo,

munthu wanzeru amafunitsitsa

kukhala ndi makutu atcheru.

Za Kuthandiza osauka

30Monga momwe madzi amazimira moto walaŵilaŵi,

momwemonso mphatso zopatsa osauka

zimapepesera machimo.

31Amene amabwezera zabwino kwa zabwino,

amaganizira zam'tsogolo.

Pamene azidzati agwe,

anzake adzamchirikiza.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help