Mas. 82 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mulungu, wolamulira wamkuluSalmo la Asafu.

1Mulungu akutsogolera msonkhano wakumwamba.

Akugamula mlandu milungu ya pansi pano.

2Akuti,

“Mudzakhalabe mukuweruza mopanda chilungamo mpaka liti?

Bwanji mukupitirizabe kumakondera anthu oipa?

3Inu tetezani anthu ofooka ndi amasiye mwachilungamo.

Weruzani molungama ozunzika ndi amphaŵi.

4“Landitsani ofooka ndi osoŵa.

Apulumutseni kwa anthu oipa.”

5Iwo sadziŵa kanthu ndiponso alibe nzeru,

amangoyenda m'chimbulimbuli.

Maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6 Yoh. 10.34 Ine ndikuti, “Inu ndinu milungu,

nonsenu ndinu ana a Mulungu Wopambanazonse.

7Komabe mudzafa ngati anthu onse,

ndipo mudzagwa ngati kalonga wina aliyense.”

8Dzambatukani, Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,

popeza kuti mitundu yonse ya anthu ndi yanu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help