Mas. 146 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nyimbo yotamanda Mulungu Mpulumutsi

1Tamandani Chauta!

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga.

2Ndidzatamanda Chauta pa moyo wanga wonse.

Ndidzaimba nyimbo zotamanda Mulungu wanga

nthaŵi zonse pamene ndili moyo.

3Musakhulupirire mafumu

kapena anthu ena amene sangathe kuthandiza.

4Pamene mpweya wa munthu uchokeratu,

munthuyo amabwerera ku dothi,

zimene ankafuna kuchita, zimatha tsiku lomwelo.

5Ngwodala munthu amene chithandizo chake

chimafumira kwa Mulungu wa Yakobe,

munthu amene amakhulupirira Chauta, Mulungu wake.

6 Ntc. 4.24; 14.15 Chauta adalenga kumwamba ndi dziko lapansi,

nyanja ndi zonse zimene zili m'menemo.

Amasunga malonjezo ake nthaŵi zonse.

7Amachitira anthu opsinjidwa zolungama,

amaŵapatsa chakudya anthu anjala.

Chauta amamasula am'ndende.

8Chauta amatsekula maso a anthu osapenya,

Chauta amakweza anthu otsitsidwa.

Chauta amakonda anthu ochita chilungamo.

9Chauta amateteza alendo,

amachirikiza mkazi wamasiye

ndiponso mwana wamasiye.

Koma njira za anthu oipa amazipotoza.

10Chauta adzakhala mfumu mpaka muyaya,

Mulungu wako, iwe Ziyoni,

adzalamulira ku mibadwo yonse.

Tamandani Chauta!

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help