Mas. 43 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pemphero la munthu wokhala ku dziko lachilendo.

1Inu Mulungu, onetsani kuti ine ndine wosalakwa,

munditchinjirize pa mlandu wanga

kwa anthu osasamala za Mulungu.

Mundipulumutse kwa anthu onyenga ndi opanda chilungamo.

2Ndithu Inu ndinu Mulungu wamphamvu

amene ndimathaĊµirako.

Mwanditayiranji?

Ndiziyenderanji ndilikulira

chifukwa chondipsinja mdani wanga?

3Tumizani kuĊµala kwanu ndi choona chanu

kuti zinditsogolere.

Zindifikitse ku phiri lanu loyera,

kumalo kokhala Inu.

4Tsono ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu,

kwa Mulungu amene amandipatsa chimwemwe chopambana.

Ndipo ndidzakutamandani ndi pangwe,

Inu Mulungu, Mulungu wanga.

5Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga?

Chifukwa chiyani ukuvutika choncho m'kati mwanga?

Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamtamandanso,

Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help