Lun. 7 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Solomoni anali munthu monga anthu ena

1Ine ndemwe ndine munthu woti ndidzafa

monga anthu ena onse.

Ndine chidzukulu cha munthu woyamba uja,

amene adampanga ndi dothi uja.

Thupi langa lidapangidwa m'mimba mwa amai anga.

2Pa miyezi khumi magazi a amaiwo

adalimbitsa thupi langali.

Ndidafumira m'mbeu ya mwamuna

ndi m'chisangalatso cha ukwati.

3Inenso nditabadwa,

ndidayamba kupuma mpweya monga wa ana onse,

ndidagwa pansi pamene amaponda anthu onse.

Ndipo monga anzanga onse,

mau anga oyamba anali olira.

4Adandifunditsa nsalu

ndi kundilera mondisamala.

5Palibe mfumu ndi imodzi yomwe

imene idaona chiyambi china cha moyo wake,

6Mabadwidwe onse ndi amodzi,

mafedwenso ndi amodzi.

Solomoni adapeza luntha pakupemphera

7 1Maf. 3.6-9; Lun. 9.1-18 Tsono ine ndidapemphera,

ndipo adandipatsa nzeru.

Ndidapemphera kwa Mulungu,

ndipo mzimu wa luntha udaloŵa mwa ine.

8Ndinkakonda luntha kupambana ndodo yaufumu

ndi mipando yachifumu,

chuma ndidachiyesa chachabe

nditachilinganiza ndi luntha.

9Sindidalilinganize ndi miyala yamtengowapatali,

chifukwa golide yense wa pansi pano

ndi kamchenga chabe pafupi ndi luntha,

ndipo siliva ali ngati fumbi

poyerekeza ndi luntha.

10Ndinkakonda luntha

kupambana moyo ndi kukongola.

Ndinkakonda kukhala nalo

kupambana kukhala ndi kuŵala kwa dzuŵa,

chifukwa kuŵala kwa lunthalo nkosalekeza.

11Zabwino zonse zidandidzera pamodzi ndi luntha,

m'luntha muli chuma chosaŵerengeka.

12Ndidakondwera nazo zabwino zonsezo,

chifukwa zidabwera ndi luntha lomwelo.

Koma sindinkadziŵa

kuti manthu wa zabwino zonsezo anali luntha.

13Monga ndidaphunzira za luntha mosadzikonda,

ndiziphunzitsanso mosamana.

Sindibisa zabwino zake,

14chifukwa luntha ndi chuma chosatha kwa anthu.

Okhala ndi lunthalo amapalana chibwenzi ndi Mulungu,

ndipo Mulungu amaŵakonda

chifukwa cha mphatso zobwera ndi luntha.

Solomoni apempha chithandizo cha Mulungu

15Mulungu andithandize kufotokoza monga kuyenera,

maganizo anga akhale oyenera mphatso

zimene ndidazilandira.

Ndiye amene amatsogolera luntha,

ndiye amene amaongolera anthu anzeru.

16Ife pamodzi ndi mau athu tili m'manja mwake,

monganso luntha lonse ndi luso logwirira ntchito.

17Ndiye amene adandipatsa nzeru

zomvetsa bwino zinthu m'mene ziliri,

ndiye amene adandidziŵitsa mapangidwe onse

a dziko lapansi ndi makhalidwe a zinthu zokhalamo.

18Ndiye amene adandiphunzitsa chiyambi,

mathero ndi mphindikati za nthaŵi,

za mayendedwe a dzuŵa

ndiponso za masinthidwe a nyengo za chaka.

19Ndiye amene adandidziŵitsa za zigawo za chaka

ndi za magulu a nyenyezi.

20Ndiye amene adandiphunzitsa

za chilengedwe cha nyama

ndi za ukali wa zilombo.

Ndiye amene adandiwuza za mphamvu za mizimu

ndi za maganizo a anthu,

ndiye amene adandiwuza za mitundu ya mbeu

ndi mphamvu za mizu yake.

21Zonse zobisika ndi zonse zodziŵikiratu ndidaphunzira,

chifukwa luntha limene lidapanga zonse

ndiye limene lidandiphunzitsa.

Ayamikira luntha

22Pajatu m'luntha muli mzimu wanzeru ndi woyera,

mzimu umodzi wokha ndi wogwira ntchito zambiri,

wosagwirika,

woyenda mwaufulu ndi woloŵerera m'zonse,

wosaipa, wapawokha, wosasinthika, wokonda zabwino,

watcheru, wosatheka kulimbana nawo.

23Mzimu umenewu ndi wachifundo,

wokonda anthu, wokhulupirika,

wosapeneka, ndi wabata,

wamphamvuzonse ndi woyang'anira zonse,

woloŵa m'mitima yonse yanzeru,

yoyera ndi yomvetsa zapatali.

24Pajatu lunthali ndi loyenda kwambiri

koposa liŵiro lina lililonse,

chifukwa chakuti ndi langwiro ndithu,

limaloŵa m'katikati mwa zinthu zonse.

25Luntha ndi mpweya wa mphamvu za Mulungu,

luntha nkunyezimira kwa ulemerero wa Wamphamvuzonse.

Nchifukwa chake koipa kalikonse sikangaloŵe m'luntha.

26Luntha nkuyera kosonyeza kuŵala kwamuyaya,

ndi kalilole kopanda maanga

koonetsa ntchito za Mulungu,

ndi chitsanzo cha ubwino wake.

27Luntha limakhoza zonse,

ngakhale lili lokha.

Limakometsanso zonse,

ngakhale ndi losasinthika.

Limaloŵa m'mitima yoyera

ya anthu a mbadwo uliwonse,

limaŵasandutsa abwenzi a Mulungu ndi aneneri.

28Pajatu amene Mulungu amaŵakonda kwambiri

ndi anthu okhala pamodzi ndi luntha.

29Pajatu luntha ndi lokongola kupambana dzuŵa,

limapambananso magulu a nyenyezi.

Limaposa kuŵala kwa usana,

30poti usiku umatsatana ndi usana,

koma zoipa sizingapambane luntha.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help