Mali. 2 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chauta alanga Yerusalemu

1Chauta wakwiya kwambiri,

taonani m'mene waphimbira Ziyoni ndi mdima!

Ulemerero wa Israele wautaya pansi kuuchotsa Kumwamba.

Pa tsiku la mkwiyo wake sadakumbukirenso

kuti Ziyoni anali ngati mphondero yake.

2Chauta adaononga midzi yonse ya Yakobe

popanda ndi chifundo chomwe.

Chifukwa cha kupsa mtima

adathyola malinga a mizinda ya Yuda.

Adagwetsera pansi mochititsa manyazi,

ufumu wa Israele ndi olamulira ake.

3Chauta atapsa mtima

adathyola nyonga zomwe ankanyadira Israele.

Adabweza dzanja lake loteteza,

adani atayandikira.

Mkwiyo wake udalanga fuko la Yakobe

ngati moto walaŵilaŵi wonka nuwononga zonse.

4Adalozetsa mivi yake kwa ife ngati mdani wathu,

wasamuladi dzanja ngati mdani.

Adapha onse amene tinkaŵayang'ana monyadira,

pakati pa anthu a mu mzinda wa Ziyoni.

Ukali wake unkachita kuyaka ngati moto.

5Chauta adakhala ngati mdani,

adaononga Israele.

Adaononga nyumba zonse zachifumu,

malinga ao onse adaŵasandutsa mabwinja.

Adachulukitsa kulira ndi kudandaula

pakati pa anthu a ku Yuda.

6Adapasula Nyumba yake ngati khumbi lam'munda,

malo ake a msonkhano adaŵasandutsa bwinja.

Chauta adathetseratu ku Ziyoni

masiku achikondwerero ndi a Sabata.

Ndipo atakwiya kwambiri

adanyoza mfumu pamodzi ndi ansembe.

7Chauta adanyoza ngakhale guwa lake lomwe,

ndipo adaŵakana malo ake opatulika.

Adapereka malinga a nyumba zake zachifumu

m'manja mwa adani ake.

M'nyumba yeniyeni ya Chauta

adaniwo adafuula ndi chimwemwe

monga momwe zimachitikira pa tsiku lachikondwerero.

8Chauta adaatsimikiza

zoti aononge malinga a mzinda wa Ziyoni.

Adauyesa ndi chingwe chake,

ndipo sadafune kuleka kuuwononga kotheratu.

Adaliritsa okhala pa malinga ndi pa makoma ake,

onsewo akuzunzikira limodzi.

9Zipata za mzindawo zakwiririka pansi.

Mipiringidzo yake yathyoka ndi kusakazika.

Mfumu yake ndi akalonga ake ali ku ukapolo

pakati pa anthu akunja,

malamulo a Mulungu palibenso oŵalalika.

Aneneri ake omwe sakuchitanso

zija zoona zinthu m'masomphenya zochokera kwa Mulungu.

10Akuluakulu a mu mzinda wa Ziyoni,

akhala pansi atangoti chete.

Adzithira fumbi kumutu, ndipo avala ziguduli.

Anamwali a ku Yerusalemu aŵeramitsa mitu yao pansi.

11Maso anga atopa nkulira,

moyo wanga wazunzika zedi,

Mumtima mwanga mwadzaza chisoni,

chifukwa choti anthu anga aonongeka,

ana ndi makanda omwe akukomoka m'miseu yamumzinda.

12Anawo akufunsa amai ao kuti,

“Kodi chakudya ndi chakumwa tingazipeze kuti?”

Akufunsa zimenezi pamene akukomoka m'miseu yamumzinda

ngati anthu olasidwa.

Akuthatha ndi moyo pa mfukato wa amai ao.

13Iwe mzinda wa Yerusalemu,

ndinganene chiyani za iwe,

kaya nkukuyerekeza ndi chiyani?

Iwe mzinda wangwiro wa Ziyoni,

kodi ndingakufanizire ndi yani,

kuti choncho ndikusangalatse?

Kuwonongeka kwako nkwakukulu ngati nyanja.

Ndani angathe kukukonzanso?

14Zinthu zimene aneneri ako adakuwonera m'masomphenya

zinali zabodza ndi zonyenga.

Iwo sadaonetse uchimo wako, kuti ukhalenso pabwino.

Mau amene adakutengeraniwo anali abodza ndi osokeretsa.

15Onse odutsa m'njira akukuwombera m'manja mokunyodola.

Akukutsonya ndi kukupukusira mitu,

iwe mzinda wa Yerusalemu.

Akunena kuti,

“Kodi mzinda uja ndi uwu

umene kale lija ankautcha wodala kotheratu,

mzinda wokondweretsa dziko lonse lapansi?”

16Adani ako onse akukuyasamira kukamwa mwaukali,

ndipo akukunyodola.

Akukutsonya ndi kumakukuta mano ao namanena kuti,

“Tafikapodi pousakaza!

Ah! Tsiku lija tinkafunali ndi lero.

Tagonera, taliwonadi.”

17Chauta wachitadi zimene adakonzekera kuti achite.

Wachitadi zimene ankanena moopseza.

Monga momwe adaakonzeratu masiku amakedzana,

wakuwononga mopanda chifundo,

walola adani kuti akondwe

chifukwa cha tsoka lako,

ndipo wakulitsa kwambiri mphamvu za adani ako.

18Fuulani kwamphamvu kwa Ambuye, inu anthu a ku Ziyoni.

Misozi yanu ichite kuti yoyoyo,

ngati mtsinje, usana ndi usiku.

Musadzipatse nthaŵi yoti mupumule.

Misozi yanu isalekeze.

19Dzukani, ndipo mufuule usiku

pachiyambi penipeni pa maulonda.

Nenani zanu zonse zakukhosi pamaso pa Ambuye.

Kwezani manja ndi kupemphera kwa Ambuyewo

chifukwa cha moyo wa ana anu

amene akukomoka ndi njala m'miseu yonse.

20Inu Chauta onani, ndipo mupenye!

Kodi ndani amene Inu mwamuvuta chotereyu?

Kodi akazi achite kudya ana ao,

ana amene iwo omwe adaŵalera bwino?

Nanga ansembe ndi aneneri,

kodi achite kuŵaphera m'malo opatulika a Ambuye?

21Anyamata ali gonegone m'miseu

pamodzi ndi nkhalamba zomwe.

Anamwali anga ndi anyamata anga aphedwa ndi nkhondo.

Mwaŵapha pa tsiku la mkwiyo wanu,

mwaŵapha mopanda chifundo.

22Monga momwe mumaitanira ku chikondwerero,

ndi m'mene mwandiitanira zoopsa kuchokera mbali zonse.

Inu Chauta, pa tsiku la mkwiyo wanu,

palibe amene adathaŵako kapena kupulumuka.

Onse amene ndidaŵabala ndi kuŵalera,

adani anga adaŵaononga.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help