Hab. 1 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1Uwu ndi uthenga umene mneneri Habakuku adalandira kwa Mulungu m'masomphenya.

Dandaulo loyamba la Habakuku

2Kodi Inu Chauta,

ndidzakhala ndikukupemphani chithandizo

nthaŵi yaitali bwanji,

Inuyo osandiyankha?

Kapena kukudandaulirani kuti “Nkhondo kuno,”

Inuyo osatipulumutsa?

3Chifukwa chiyani mukufuna

kuti ndiziwona mavuto otereŵa.

Chifukwa chiyani mukulekerera zoipa?

Ponseponse ndikuwona chiwonongeko ndiponso nkhondo.

Pali ndeu ndi kukangana kwambiri.

4Ndiye kuti malamulo atha mphamvu.

Chilungamo sichikugwira ntchito.

Anthu oipa akupambana anthu abwino,

motero chilungamo chalephereka.

Yankho la Chauta

5 Ntc. 13.41 Onani mitundu ya anthuyi, muipenyetsetse.

Kudzakhala zododometsa ndipo mudzangoti kakasi.

Pakuti ndidzachita zinthu

zimene simudzakhulupirira mukadzazimva.

6 2Maf. 24.2 Ndiye kuti ndidzakweza Ababiloni

mtundu woopsa ndi wamphamvu.

Iwowo amapita pa dziko lonse lapansi

kuti akalande malo a eniake.

7Kulikonse kumene amapita, amachititsa mantha,

amadzipangira okha malamulo,

amadzipezera okha ulemu.

8Akavalo ao ndi aliŵiro kwambiri kupambana akambuku,

ndi oopsa kupambana mimbulu yolusa.

Okwerapo ao akuthamanga molunjika kuchokera kutali.

Akuchita kugudukira ngati chiwombankhanga

chofuna kugwira nyama.

9Gulu lao lankhondo likubwera ndi nkhanza,

anthu akuchita mantha iwo asanafike.

Amagwira akapolo ochuluka ngati mchenga.

10Amanyoza mafumu,

amanyazitsa atsogoleri.

Amapeputsa linga lililonse,

poti amangounjika dothi lokwererapo,

nalanda mzinda wake.

11Kenaka amapitirira mofulumira ngati mphepo.

Anthuwo amene mphamvu ndiye mulungu wao.

Dandaulo lachiŵiri la Habakuku

12Inu Chauta, kodi suja ndinu wachikhalire?

Ndinu Mulungu wanga, Woyera wanga uja, wosafa.

Inu Chauta, ndinu amene mudaŵasankha anthuwo

kuti abweretse chiweruzo pa ife.

Inu Thanthwe lathu, mudaŵaika iwowo kuti atilange.

13Maso anu ndi oyera, safuna kuwona zoipa,

simungalekerere anthu ochita uchimo ndi zolakwa.

Chifukwa chiyani nanga mukulekerera

anthu osakhulupirikawo?

Bwanji simuchitapo kanthu

pamene anthu oipa akuwononga anthu abwino

kupambana iwowo?

14Mumasandutsa anthu kuti azikhala

ngati nsomba zam'nyanja,

ngati zokwaŵa zimene zilibe wozilamulira?

15Adani ao amachita ngati kuŵedza anthuwo ndi mbedza,

kapena kuŵakola m'kombe.

Amaŵakokera m'matchera ao,

ndipo amakondwa ndi kusangalala.

16Tsono amaperekera nsembe makombe ao,

ndipo amafukizira lubani matchera ao.

Chifukwa zimenezi ndizo zimaŵabweretsera

moyo wapamwamba, ndipo amadya bwino.

17Kodi adzapitirirabe kugwiritsa ntchito makoka ao,

ndi kumapha mitundu ya anthu mopanda

chifundo mpakampaka?

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help