Mas. 2 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mfumu yodzozedwa ya Mulungu

1 Ntc. 4.25, 26 Bwanji anthu akunja

akufuna kuchita chiwembu?

Chifukwa chiyani anthu ameneŵa

akulingalira zopandapake?

2Mafumu ao akuchita upo,

olamula ao akhala pamodzi kuti apangane zoipa,

zoukira Chauta ndi mfumu yake yodzozedwa.

3Akuti,

“Tiyeni timasule maunyolo aoŵa,

tichokeretu mu ulamuliro wao.”

4Chauta amene amalamulira kumwambako

akungoŵaseka ndi kuŵanyoza.

5Tsono adzaŵadzudzula ali wokwiya

adzaŵaopseza ali wokalipa.

6Adzati,

“Ine ndakhazika kale mfumu yanga,

ili pa phiri langa loyera la Ziyoni.”

7 Ntc. 13.33; Ahe. 1.5; 5.5 Tsono mfumuyo ikuti,

“Ndidzalalika zimene Chauta walengeza.

Adandiwuza kuti,

‘Iwe ndiwe mwana wanga,

Ine lero ndakubala.

8Tandipempha uwone,

ndidzasandutsadi mitundu ya anthu

kuti ikhale choloŵa chako,

ndipo dziko lonse lapansi lidzakhala lako.

9 Chiv. 2.26, 27; 12.5; 19.15 Udzaŵaphwanya ndi ndodo yachitsulo,

ndi kuŵatekedza zidutswazidutswa monga mbiya.’ ”

10Nchifukwa chake tsono khalani anzeru,

inu mafumu.

Chenjerani inu amene muli olamula dziko lapansi.

11Tumikirani Chauta mwamantha ndi monjenjemera.

12Mumgonjere molapa,

kuwopa kuti angakukwiyireni,

ndipo inu mungaonongeke,

chifukwa ukali wake umayaka msanga.

Ngodala onse amene amathaŵira kwa Iye.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help