Mphu. 44 - Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

B: M'MBIRI YAKALEKulemekeza makolo athu akale ku Israele

1Tsopano tiyeni titamande anthu otchuka

ndi kunyadira makolo athu potsata mibadwo yao.

2Mulungu adaonetsa mwa iwo kukula kwa ulemerero wake,

ndipo adasonyeza ukulu wake chiyambire.

3Ena adakhala mafumu m'maiko ao,

ndipo adatchuka chifukwa cha mphamvu zao.

Ena anali aphungu anzeru

ndipo ankalankhula zolosa.

4Ena ankatsogolera anthu ndi malangizo ao,

ankamvetsa bwino za m'mitima mwa anthu,

ndipo ankaphunzitsa anthu ao mwanzeru.

5Ena anali opeka nyimbo zokoma

ndipo ankalemba ndakatulo.

6Ena anali olemera ndi amphamvu,

ankakhala mwamtendere m'nyumba mwao.

7Anthu onseŵa adatchuka pakati pa anthu a mbadwo wao,

ndipo ankaŵanyadira pa moyo wao.

8Ena adasiya mbiri yabwino,

ndipo anthu akuŵakumbukirabe mpaka pano.

9Pali ena amene anthu saŵakumbukira,

amene adangoti zii, ngati sadakhalepo ndi moyo.

Iwo achita ngati sadabadwe konse,

chimodzimodzinso ana ao oŵatsatira.

10Koma nawu mndandanda wa anthu otchuka,

amene ntchito zao zabwino siziiŵalika.

11Chuma chao adzachilandira ndi ana ao,

ndipo choloŵa chao chidzakhala cha mibadwo yakutsogolo.

12Ana ao amasungabe chipangano,

zidzukulu zao zidzateronso chifukwa cha makolo ao.

13Zidzukulu zao zidzakhala mpaka muyaya,

ndipo ulemerero wao sudzazimirira.

14Mitembo yao adaiika mwamtendere,

koma mbiri yao idzakhala mpaka muyaya.

15Mitundu ya anthu idzalalika nzeru za anthu ameneŵa,

ndipo anthu a Mulungu adzaimba nyimbo zoŵatamanda.

Enoki

16 Gen. 5.24; Ahe. 11.5; Yuda 1.14 Enoki adakondwetsa Ambuye, ndipo adatengedwa

kupita kumwamba.

Iye adapatsa mibadwo yonse chitsanzo cha

kutembenuka mtima.

Nowa

17 Gen. 6.9—9.17 Nowa adapezeka kuti anali munthu wangwiro

ndi wolungama.

Pa nthaŵi ya chilango iye adakhala ngati chiphukira,

chifukwa cha iye pa nthaŵi ya chigumula

padatsalira anthu ena pansi pano.

18Ambuye adachita naye chipangano chamuyaya

chakuti zamoyo zonse sizidzaonongekanso ndi chigumula.

Abrahamu

19 Gen. 15.1—17.27; 22.1-18 Abrahamu anali kholo lotchuka la mitundu

yambiri ya anthu.

Palibe amene adakhala womveka ngati iyeyo.

20Adatsata malamulo a Mulungu Wopambanazonse,

ndipo adachita naye chipangano.

Adakhazikitsa chipanganocho m'thupi mwake,

ndipo atamuyesa, adampeza kuti ali wokhulupirika.

21Nchifukwa chake Ambuye adamlonjeza molumbira

kuti adzadalitsa mitundu ya anthu mwa zidzukulu zake,

ndiponso kuti zidzukulu zakezo zidzachuluka

ngati fumbi la pa dziko lapansi,

zidzakwezedwa ngati nyenyezi.

Adalonjezanso kuti dziko laolo lidzakhala lalikuludi,

kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina,

ndiponso kuchokera ku mtsinje waukulu mpaka

ku malire a dziko lapansi.

Isaki ndi Yakobe

22 Gen. 17.19; 26.3-5; 27.28; 28.14 Isakinso adamlonjeza zomwezo

chifukwa cha bambo wake Abrahamu.

23Madalitso oyenerera mtundu wonse wa anthu ndi chipangano,

adazigoneka pa Yakobe.

Adamlimbitsa m'madalitso amene adampatsawo

ndipo adampatsa dziko kuti likhale choloŵa chake.

Adaliduladula m'zigawo

naligaŵira mafuko khumi ndi aŵiri aja.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help